< 2 Kings 3 >
1 And Jehoram, the son of Ahab, became king over Israel in Samaria in the eighteenth year of the rule of Jehoshaphat, king of Judah; and he was king for twelve years.
Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
2 He did evil in the eyes of the Lord; but not like his father and his mother, for he put away the stone pillar of Baal which his father had made.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
3 But still he did the same sins which Jeroboam, the son of Nebat, did and made Israel do; he went on in them.
Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
4 Now Mesha, king of Moab, was a sheep-farmer; and he gave regularly to the king of Israel the wool from a hundred thousand lambs and a hundred thousand sheep.
Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
5 But when Ahab was dead, the king of Moab got free from the authority of the king of Israel.
Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
6 At that time, King Jehoram went out from Samaria and got all Israel together in fighting order.
Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
7 And he sent to Jehoshaphat, king of Judah, saying, The king of Moab has got free from my authority: will you go with me to make war on Moab? And he said, I will go with you: I am as you are, my people as your people, and my horses as your horses.
Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
8 And he said, Which way are we to go? And he said in answer, By the waste land of Edom.
Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
9 So the king of Israel went with the king of Judah and the king of Edom by a roundabout way for seven days: and there was no water for the army or for the beasts they had with them.
Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
10 And the king of Israel said, Here is trouble: for the Lord has got these three kings together to give them into the hands of Moab.
Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
11 But Jehoshaphat said, Is there no prophet of the Lord here, through whom we may get directions from the Lord? And one of the king of Israel's men said in answer, Elisha, the son of Shaphat, is here, who was servant to Elijah.
Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
12 And Jehoshaphat said, The word of the Lord is with him. So the king of Israel and Jehoshaphat and the king of Edom went down to him.
Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
13 But Elisha said to the king of Israel, What have I to do with you? go to the prophets of your father and your mother. And the king of Israel said, No; for the Lord has got these three kings together to give them up into the hands of Moab.
Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
14 Then Elisha said, By the life of the Lord of armies whose servant I am, if it was not for the respect I have for Jehoshaphat, king of Judah, I would not give a look at you, or see you.
Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
15 But now, get me a player of music, and it will come about that while the man is playing, the hand of the Lord will come on me and I will give you the word of the Lord: and they got a player of music, and while the man was playing, the hand of the Lord was on him.
Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
16 And he said, The Lord says, I will make this valley full of water-holes.
ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
17 For the Lord says, Though you see no wind or rain, the valley will be full of water, and you and your armies and your beasts will have drink.
Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
18 And this will be only a small thing to the Lord: in addition he will give the Moabites into your hands.
Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
19 And you are to put every walled town to destruction, cutting down every good tree, and stopping up every water-spring, and making all the good land rough with stones.
Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
20 Now in the morning, about the time when the offering was made, they saw water flowing from the direction of Edom till the country was full of water.
Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
21 Now all Moab, hearing that the kings had come to make war against them, got together all who were able to take up arms and went forward to the edge of the country.
Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
22 And early in the morning they got up, when the sun was shining on the water, and they saw the water facing them as red as blood.
Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
23 Then they said, This is blood: it is clear that destruction has come on the kings; they have been fighting one another: now come, Moab, let us take their goods.
Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
24 But when they came to the tents of Israel, the Israelites came out and made a violent attack on the Moabites, so that they went in flight before them; and they went forward still attacking them;
Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
25 Pulling down the towns, covering every good field with stones, stopping up all the water-springs, and cutting down all the good trees; they went on driving Moab before them till only in Kir-hareseth were there any Moabites; and the fighting-men went round the town raining stones on it.
Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
26 And when the king of Moab saw that the fight was going against him, he took with him seven hundred men armed with swords, with the idea of forcing a way through to the king of Aram, but they were not able to do so.
Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
27 Then he took his oldest son, who would have been king after him, offering him as a burned offering on the wall. So there was great wrath against Israel; and they went away from him, back to their country.
Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.