< 2 Chronicles 29 >

1 Hezekiah became king when he was twenty-five years old; and he was king in Jerusalem for twenty-nine years; and his mother's name was Abijah, the daughter of Zechariah.
Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
2 He did what was right in the eyes of the Lord, as his father David had done.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
3 In the first year of his rule, in the first month, opening the doors of the Lord's house, he made them strong.
Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
4 And he sent for the priests and the Levites, and got them together in the wide place on the east side,
Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
5 And said to them, Give ear to me, O Levites: now make yourselves holy, and make holy the house of the Lord, the God of your fathers, and take away everything unclean from the holy place.
ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
6 For our fathers have done evil, sinning in the eyes of the Lord our God, and have given him up, turning away their faces from the house of the Lord, and turning their backs on him.
Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
7 The doors of his house have been shut and the lights put out; no perfumes have been burned or offerings made to the God of Israel in his holy place.
Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
8 And so the wrath of the Lord has come on Judah and Jerusalem, and he has given them up to be a cause of fear and wonder and shame, as your eyes have seen.
Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
9 For see, our fathers have been put to death with the sword, and our sons and daughters and wives have been taken away prisoners because of this.
Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
10 Now it is my purpose to make an agreement with the Lord, the God of Israel, so that the heat of his wrath may be turned away from us.
Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
11 My sons, take care now: for you have been marked out by the Lord to come before him and to be his servants, burning offerings to him.
Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
12 Then the Levites took their places; Mahath, the son of Amasai, and Joel, the son of Azariah, among the Kohathites; and of the sons of Merari, Kish, the son of Abdi, and Azariah, the son of Jehallelel; and of the Gershonites, Joah, the son of Zimmah, and Eden, the son of Joah;
Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
13 And of the sons of Elizaphan, Shimri and Jeuel; and of the sons of Asaph, Zechariah and Mattaniah;
kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
14 And of the sons of Heman, Jehuel and Shimei; and of the sons of Jeduthun, Shemaiah and Uzziel.
kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
15 And they got their brothers together and made themselves holy, and went in, as the king had said by the word of the Lord, to make the house of the Lord clean.
Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
16 And the priests went into the inner part of the house of the Lord to make it clean, and everything unclean which was to be seen in the Temple of the Lord they took out into the outer square of the Lord's house, and the Levites got it together and took it away to the stream Kidron.
Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
17 On the first day of the first month the work of making the house holy was started, and on the eighth day they came to the covered way of the Lord; in eight days they made the Lord's house holy, and on the sixteenth day of the first month the work was done.
Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
18 Then they went in to King Hezekiah and said, We have made all the house of the Lord clean, as well as the altar of burned offerings with all its vessels, and the table for the holy bread, with all its vessels.
Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
19 And all the vessels which were turned out by King Ahaz in his sin while he was king, we have put in order and made holy, and now they are in their places before the altar of the Lord.
Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
20 Then Hezekiah the king got up early, and got together the great men of the town, and went up to the house of the Lord.
Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
21 And they took with them seven oxen and seven male sheep and seven lambs and seven he-goats as a sin-offering for the kingdom and for the holy house and for Judah. And he gave orders to the sons of Aaron, the priests, that these were to be offered on the altar of the Lord.
Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
22 So they put the oxen to death and their blood was given to the priests to be drained out against the altar; then they put the male sheep to death, draining out their blood against the altar, and they put the lambs to death, draining out their blood against the altar.
Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
23 Then they took the he-goats for the sin-offering, placing them before the king and the meeting of the people, and they put their hands on them:
Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
24 And the priests put them to death, and made a sin-offering with their blood on the altar, to take away the sin of all Israel: for the king gave orders that the burned offering and the sin-offering were for all Israel.
Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
25 Then he put the Levites in their places in the house of the Lord, with brass and corded instruments of music as ordered by David and Gad, the king's seer, and Nathan the prophet: for the order was the Lord's, given by his prophets.
Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
26 So the Levites took their places with David's instruments, and the priests with their horns.
Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
27 And Hezekiah gave the word for the burned offering to be offered on the altar. And when the burned offering was started, then the song of the Lord was started, with the blowing of horns and with all the instruments of David, king of Israel.
Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
28 And all the people gave worship, to the sound of songs and the blowing of horns; and this went on till the burned offering was ended.
Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
29 And at the end of the offering, the king and all who were present with him gave worship with bent heads.
Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
30 Then King Hezekiah and the captains gave orders to the Levites to give praise to God in the words of David and Asaph the seer. And they made songs of praise with joy, and with bent heads gave worship.
Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
31 Then Hezekiah made answer and said, Now that you have given yourselves to the Lord, come near and take offerings and praise-offerings into the house of the Lord. So all the people took in offerings and praise-offerings: and those whose hearts were moved, took in burned offerings.
Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
32 The number of burned offerings which the people took in was seventy oxen, a hundred male sheep, and two hundred lambs: all these were for burned offerings to the Lord.
Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
33 And the holy things were six hundred oxen and three thousand sheep.
Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
34 There were not enough priests for the work of cutting up all the burned offerings; so their brothers the Levites gave them help till the work was done and the priests had made themselves holy: for the Levites were more upright in heart to make themselves holy than the priests.
Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
35 And there was a great amount of burned offerings, with the fat of the peace-offerings and the drink offerings for every burned offering. So the work of the Lord's house was put in order.
Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
36 And Hezekiah and all the people were full of joy, because God had made the people ready: for the thing was done suddenly.
Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

< 2 Chronicles 29 >