< 1 Samuel 11 >
1 Then about a month after this, Nahash the Ammonite came up and put his forces in position for attacking Jabesh-gilead: and all the men of Jabesh said to Nahash, Make an agreement with us and we will be your servants.
Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
2 And Nahash the Ammonite said to them, I will make an agreement with you on this condition, that all your right eyes are put out; so that I may make it a cause of shame to all Israel.
Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
3 Then the responsible men of Jabesh said to him, Give us seven days, so that we may send men to every part of Israel: and then, if no one comes to our help, we will come out to you.
Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
4 So they sent representatives to Saul's town Gibeah, and these gave the news to the people: and all the people gave themselves to weeping.
Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
5 Now Saul came from the field, driving the oxen before him; and he said, Why are the people weeping? And they gave him word of what the men of Jabesh had said.
Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
6 And at their words, the spirit of God came on Saul with power, and he became very angry.
Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
7 And he took two oxen and, cutting them up, sent them through all the land of Israel by the hand of runners, saying, If any man does not come out after Saul and Samuel, this will be done to his oxen. And the fear of the Lord came on the people and they came out like one man.
Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
8 And he had them numbered in Bezek: the children of Israel were three hundred thousand, and the men of Judah thirty thousand.
Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
9 Then he said to the representatives who had come, Say to the men of Jabesh-gilead, Tomorrow, by the time the sun is high, you will be made safe. And the representatives came and gave the news to the men of Jabesh; and they were glad.
Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
10 So the men of Jabesh said, Tomorrow we will come out to you, and you may do to us whatever seems good to you.
Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
11 Now on the day after, Saul put the people into three bands, and in the morning watch they came to the tents of the Ammonites, and they went on attacking them till the heat of the day: and those who were not put to death were put to flight in every direction, so that no two of them were together.
Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
12 And the people said to Samuel, Who was it who said, Is Saul to be our king? give the men up, so that we may put them to death.
Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
13 And Saul said, Not a man is to be put to death today: for today the Lord has made Israel safe.
Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
14 Then Samuel said to the people, Come, let us go to Gilgal and there make the kingdom strong in the hands of Saul.
Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
15 So all the people went to Gilgal; and there in Gilgal they made Saul king before the Lord; and peace-offerings were offered before the Lord; and there Saul and all the men of Israel were glad with great joy.
Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.