< 1 Chronicles 18 >
1 And it came about after this that David made an attack on the Philistines and overcame them, and took Gath with its daughter-towns out of the hands of the Philistines.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 And he overcame Moab, and the Moabites became his servants and gave him offerings.
Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
3 Then David overcame Hadadezer, king of Zobah, near Hamath, when he was going to make his power seen by the river Euphrates.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 And David took from him a thousand war-carriages and seven thousand horsemen and twenty thousand footmen: and he had the leg-muscles of all the horses cut, keeping only enough of them for a hundred war-carriages.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 And when the Aramaeans of Damascus came to the help of Hadadezer, king of Zobah, David put to the sword twenty-two thousand Aramaeans.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 Then David put armed forces in Damascus, and the Aramaeans became his servants and gave him offerings. And the Lord made David overcome wherever he went.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 And the gold body-covers of the servants of Hadadezer, David took to Jerusalem.
Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 And from Tibhath and from Cun, towns of Hadadezer, David took a great store of brass, of which Solomon made the great brass water-vessel and the brass pillars and vessels.
Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
9 Now when Tou, king of Hamath, had news that David had overcome all the army of Hadadezer, king of Zobah,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
10 He sent his son Hadoram to King David, to give him words of peace and blessing, because he had overcome Hadadezer in the fight, for Hadadezer had been at war with Tou; and he gave him all sorts of vessels of gold and silver and brass.
anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
11 These King David made holy to the Lord, together with the silver and gold he had taken from all nations; from Edom and Moab and from the children of Ammon and from the Philistines and from Amalek.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
12 And when he came back from putting to the sword eighteen thousand of the Edomites in the Valley of Salt,
Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
13 David put armed forces in all the towns of Edom; and all the Edomites became servants to David. The Lord made David overcome wherever he went.
Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
14 So David was king over all Israel, judging and giving right decisions for all his people.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
15 And Joab, the son of Zeruiah, was chief of the army; and Jehoshaphat, son of Ahilud, was keeper of the records.
Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
16 And Zadok, the son of Ahitub; and Ahimelech, the son of Abiathar, were priests; and Shavsha was the scribe;
Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
17 And Benaiah, the son of Jehoiada, was over the Cherethites and the Pelethites; and the sons of David were chief of those whose places were at the king's side.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.