< Psalms 75 >

1 For the choirmaster: To the tune of “Do Not Destroy.” A Psalm of Asaph. A song. We give thanks to You, O God; we give thanks, for Your Name is near. The people declare Your wondrous works.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 “When I choose a time, I will judge fairly.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 When the earth and all its dwellers quake, it is I who bear up its pillars.
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 I say to the proud, ‘Do not boast,’ and to the wicked, ‘Do not lift up your horn.
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Do not lift up your horn against heaven or speak with an outstretched neck.’”
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 For exaltation comes neither from east nor west, nor out of the desert,
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 but it is God who judges; He brings down one and exalts another.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 For a cup is in the hand of the LORD, full of foaming wine mixed with spices. He pours from His cup, and all the wicked of the earth drink it down to the dregs.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 But I will proclaim Him forever; I will sing praise to the God of Jacob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 “All the horns of the wicked I will cut off, but the horns of the righteous will be exalted.”
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalms 75 >