< Psalms 50 >

1 A Psalm of Asaph. The Mighty One, God the LORD, speaks and summons the earth from where the sun rises to where it sets.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 From Zion, perfect in beauty, God shines forth.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Our God approaches and will not be silent! Consuming fire precedes Him, and a tempest rages around Him.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 He summons the heavens above, and the earth, that He may judge His people:
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 “Gather to Me My saints, who made a covenant with Me by sacrifice.”
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 And the heavens proclaim His righteousness, for God Himself is Judge.
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 “Hear, O My people, and I will speak, O Israel, and I will testify against you: I am God, your God.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 I do not rebuke you for your sacrifices, and your burnt offerings are ever before Me.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 I have no need for a bull from your stall or goats from your pens,
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 for every beast of the forest is Mine— the cattle on a thousand hills.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 I know every bird in the mountains, and the creatures of the field are Mine.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 If I were hungry, I would not tell you, for the world is Mine, and the fullness thereof.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Do I eat the flesh of bulls, or drink the blood of goats?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Sacrifice a thank offering to God, and fulfill your vows to the Most High.
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 Call upon Me in the day of trouble; I will deliver you, and you will honor Me.”
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 To the wicked, however, God says, “What right have you to recite My statutes and to bear My covenant on your lips?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 For you hate My instruction and cast My words behind you.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 When you see a thief, you befriend him, and throw in your lot with adulterers.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 You unleash your mouth for evil and unharness your tongue for deceit.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 You sit and malign your brother; you slander your own mother’s son.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 You have done these things, and I kept silent; you thought I was just like you. But now I rebuke you and accuse you to your face.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Now consider this, you who forget God, lest I tear you to pieces, with no one to rescue you:
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 He who sacrifices a thank offering honors Me, and to him who rights his way, I will show the salvation of God.”
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psalms 50 >