< Psalms 3 >

1 A Psalm of David, when he fled from his son Absalom. O LORD, how my foes have increased! How many rise up against me!
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 Many say of me, “God will not deliver him.”
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 But You, O LORD, are a shield around me, my glory, and the One who lifts my head.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 To the LORD I cry aloud, and He answers me from His holy mountain.
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 I lie down and sleep; I wake again, for the LORD sustains me.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 I will not fear the myriads set against me on every side.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Arise, O LORD! Save me, O my God! Strike all my enemies on the jaw; break the teeth of the wicked.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 Salvation belongs to the LORD; may Your blessing be on Your people.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Psalms 3 >