< Psalms 18 >
1 For the choirmaster. Of David the servant of the LORD, who sang this song to the LORD on the day the LORD had delivered him from the hand of all his enemies and from the hand of Saul. He said: I love You, O LORD, my strength.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 The LORD is my rock, my fortress, and my deliverer. My God is my rock, in whom I take refuge, my shield, and the horn of my salvation, my stronghold.
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 I will call upon the LORD, who is worthy to be praised; so shall I be saved from my enemies.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 The cords of death encompassed me; the torrents of chaos overwhelmed me.
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 The cords of Sheol entangled me; the snares of death confronted me. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
6 In my distress I called upon the LORD; I cried to my God for help. From His temple He heard my voice, and my cry for His help reached His ears.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 Then the earth shook and quaked, and the foundations of the mountains trembled; they were shaken because He burned with anger.
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 Smoke rose from His nostrils, and consuming fire came from His mouth; glowing coals blazed forth.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 He parted the heavens and came down with dark clouds beneath His feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 He mounted a cherub and flew; He soared on the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 He made darkness His hiding place, and storm clouds a canopy around Him.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 From the brightness of His presence His clouds advanced— hailstones and coals of fire.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 The LORD thundered from heaven; the voice of the Most High resounded— hailstones and coals of fire.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 He shot His arrows and scattered the foes; He hurled lightning and routed them.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 The channels of the sea appeared, and the foundations of the world were exposed, at Your rebuke, O LORD, at the blast of the breath of Your nostrils.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 He reached down from on high and took hold of me; He drew me out of deep waters.
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 He rescued me from my powerful enemy, from foes too mighty for me.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 They confronted me in my day of calamity, but the LORD was my support.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 He brought me out into the open; He rescued me because He delighted in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 The LORD has rewarded me according to my righteousness; He has repaid me according to the cleanness of my hands.
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 For I have kept the ways of the LORD and have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 For all His ordinances are before me; I have not disregarded His statutes.
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 And I have been blameless before Him and kept myself from iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 So the LORD has repaid me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in His sight.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 To the faithful You show Yourself faithful, to the blameless You show Yourself blameless;
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 to the pure You show Yourself pure, but to the crooked You show Yourself shrewd.
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 For You save an afflicted people, but You humble those with haughty eyes.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 For You, O LORD, light my lamp; my God lights up my darkness.
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 For in You I can charge an army, and with my God I can scale a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 As for God, His way is perfect; the word of the LORD is flawless. He is a shield to all who take refuge in Him.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 For who is God besides the LORD? And who is the Rock except our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 It is God who arms me with strength and makes my way clear.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 He makes my feet like those of a deer and stations me upon the heights.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 He trains my hands for battle; my arms can bend a bow of bronze.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 You have given me Your shield of salvation; Your right hand upholds me, and Your gentleness exalts me.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 You broaden the path beneath me so that my ankles do not give way.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 I pursued my enemies and overtook them; I did not turn back until they were consumed.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 I crushed them so they could not rise; they have fallen under my feet.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 You have armed me with strength for battle; You have subdued my foes beneath me.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 You have made my enemies retreat before me; I put an end to those who hated me.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 They cried for help, but there was no one to save them— to the LORD, but He did not answer.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 I ground them as dust in the face of the wind; I trampled them like mud in the streets.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 You have delivered me from the strife of the people; You have made me the head of nations; a people I had not known shall serve me.
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 When they hear me, they obey me; foreigners cower before me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 Foreigners lose heart and come trembling from their strongholds.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 The LORD lives, and blessed be my Rock! And may the God of my salvation be exalted—
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 the God who avenges me and subdues nations beneath me,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 who delivers me from my enemies. You exalt me above my foes; You rescue me from violent men.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 Therefore I will praise You, O LORD, among the nations; I will sing praises to Your name.
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 Great salvation He brings to His king. He shows loving devotion to His anointed, to David and his descendants forever.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.