< Psalms 147 >

1 Hallelujah! How good it is to sing praises to our God, how pleasant and lovely to praise Him!
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 The LORD builds up Jerusalem; He gathers the exiles of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 He heals the brokenhearted and binds up their wounds.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 He determines the number of the stars; He calls them each by name.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Great is our Lord, and mighty in power; His understanding has no limit.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 The LORD sustains the humble, but casts the wicked to the ground.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Sing to the LORD with thanksgiving; make music on the harp to our God,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 who covers the sky with clouds, who prepares rain for the earth, who makes grass to grow on the hills.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 He provides food for the animals, and for the young ravens when they call.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He does not delight in the strength of the horse; He takes no pleasure in the legpower of the man.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 The LORD is pleased with those who fear Him, who hope in His loving devotion.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Exalt the LORD, O Jerusalem; praise your God, O Zion!
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For He strengthens the bars of your gates and blesses the children within you.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 He makes peace at your borders; He fills you with the finest wheat.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 He sends forth His command to the earth; His word runs swiftly.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 He spreads the snow like wool; He scatters the frost like ashes;
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He casts forth His hail like pebbles. Who can withstand His icy blast?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He sends forth His word and melts them; He unleashes His winds, and the waters flow.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 He declares His word to Jacob, His statutes and judgments to Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He has done this for no other nation; they do not know His judgments. Hallelujah!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 147 >