< Psalms 129 >
1 A song of ascents. Many a time they have persecuted me from my youth— let Israel now declare—
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 many a time they have persecuted me from my youth, but they have not prevailed against me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 The plowmen plowed over my back; they made their furrows long.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 The LORD is righteous; He has cut me from the cords of the wicked.
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 May all who hate Zion be turned back in shame.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 May they be like grass on the rooftops, which withers before it can grow,
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 unable to fill the hands of the reaper, or the arms of the binder of sheaves.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 May none who pass by say to them, “The blessing of the LORD be on you; we bless you in the name of the LORD.”
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”