< Psalms 124 >

1 A song of ascents. Of David. If the LORD had not been on our side— let Israel now declare—
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
2 if the LORD had not been on our side when men attacked us,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
3 when their anger flared against us, then they would have swallowed us alive,
iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
4 then the floods would have engulfed us, then the torrent would have overwhelmed us,
chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
5 then the raging waters would have swept us away.
madzi a mkokomo akanatikokolola.
6 Blessed be the LORD, who has not given us as prey to their teeth.
Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 We have escaped like a bird from the snare of the fowler; the net is torn, and we have slipped away.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
8 Our help is in the name of the LORD, the Maker of heaven and earth.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

< Psalms 124 >