< Psalms 119 >

1 Blessed are those whose way is blameless, who walk in the Law of the LORD.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Blessed are those who keep His testimonies and seek Him with all their heart.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 They do no iniquity; they walk in His ways.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 You have ordained Your precepts, that we should keep them diligently.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oh, that my ways were committed to keeping Your statutes!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Then I would not be ashamed when I consider all Your commandments.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I will praise You with an upright heart when I learn Your righteous judgments.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 I will keep Your statutes; do not utterly forsake me.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 How can a young man keep his way pure? By guarding it according to Your word.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 With all my heart I have sought You; do not let me stray from Your commandments.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 I have hidden Your word in my heart that I might not sin against You.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Blessed are You, O LORD; teach me Your statutes.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 With my lips I proclaim all the judgments of Your mouth.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 I rejoice in the way of Your testimonies as much as in all riches.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 I will meditate on Your precepts and regard Your ways.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 I will delight in Your statutes; I will not forget Your word.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Deal bountifully with Your servant, that I may live and keep Your word.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Open my eyes that I may see wondrous things from Your law.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 I am a stranger on the earth; do not hide Your commandments from me.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 My soul is consumed with longing for Your judgments at all times.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 You rebuke the arrogant— the cursed who stray from Your commandments.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Remove my scorn and contempt, for I have kept Your testimonies.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Though rulers sit and slander me, Your servant meditates on Your statutes.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Your testimonies are indeed my delight; they are my counselors.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 My soul cleaves to the dust; revive me according to Your word.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 I recounted my ways, and You answered me; teach me Your statutes.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Make clear to me the way of Your precepts; then I will meditate on Your wonders.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 My soul melts with sorrow; strengthen me according to Your word.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Remove me from the path of deceit and graciously grant me Your law.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 I have chosen the way of truth; I have set Your ordinances before me.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 I cling to Your testimonies, O LORD; let me not be put to shame.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 I run in the path of Your commandments, for You will enlarge my heart.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Teach me, O LORD, the way of Your statutes, and I will keep them to the end.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Give me understanding that I may obey Your law, and follow it with all my heart.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Direct me in the path of Your commandments, for there I find delight.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Turn my heart to Your testimonies and not to covetous gain.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Turn my eyes away from worthless things; revive me with Your word.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Establish Your word to Your servant, to produce reverence for You.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Turn away the disgrace I dread, for Your judgments are good.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 How I long for Your precepts! Revive me in Your righteousness.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 May Your loving devotion come to me, O LORD, Your salvation, according to Your promise.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Then I can answer him who taunts, for I trust in Your word.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Never take Your word of truth from my mouth, for I hope in Your judgments.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 I will always obey Your law, forever and ever.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 And I will walk in freedom, for I have sought Your precepts.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 I will speak of Your testimonies before kings, and I will not be ashamed.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 I delight in Your commandments because I love them.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 I lift up my hands to Your commandments, which I love, and I meditate on Your statutes.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Remember Your word to Your servant, upon which You have given me hope.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 This is my comfort in affliction, that Your promise has given me life.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 The arrogant utterly deride me, but I do not turn from Your law.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 I remember Your judgments of old, O LORD, and in them I find comfort.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Rage has taken hold of me because of the wicked who reject Your law.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Your statutes are songs to me in the house of my pilgrimage.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 In the night, O LORD, I remember Your name, that I may keep Your law.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This is my practice, for I obey Your precepts.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 The LORD is my portion; I have promised to keep Your words.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I have sought Your face with all my heart; be gracious to me according to Your promise.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I considered my ways and turned my steps to Your testimonies.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I hurried without hesitating to keep Your commandments.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Though the ropes of the wicked bind me, I do not forget Your law.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 At midnight I rise to give You thanks for Your righteous judgments.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 I am a friend to all who fear You, and to those who keep Your precepts.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 The earth is filled with Your loving devotion, O LORD; teach me Your statutes.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 You are good to Your servant, O LORD, according to Your word.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Teach me good judgment and knowledge, for I believe in Your commandments.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Before I was afflicted, I went astray; but now I keep Your word.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 You are good, and You do what is good; teach me Your statutes.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Though the arrogant have smeared me with lies, I keep Your precepts with all my heart.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Their hearts are hard and callous, but I delight in Your law.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It was good for me to be afflicted, that I might learn Your statutes.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 The law from Your mouth is more precious to me than thousands of pieces of gold and silver.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Your hands have made me and fashioned me; give me understanding to learn Your commandments.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 May those who fear You see me and rejoice, for I have hoped in Your word.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 I know, O LORD, that Your judgments are righteous, and that in faithfulness You have afflicted me.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 May Your loving devotion comfort me, I pray, according to Your promise to Your servant.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 May Your compassion come to me, that I may live, for Your law is my delight.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 May the arrogant be put to shame for subverting me with a lie; I will meditate on Your precepts.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 May those who fear You turn to me, those who know Your testimonies.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 May my heart be blameless in Your statutes, that I may not be put to shame.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 My soul faints for Your salvation; I wait for Your word.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 My eyes fail, looking for Your promise; I ask, “When will You comfort me?”
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Though I am like a wineskin dried up by smoke, I do not forget Your statutes.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 How many days must Your servant wait? When will You execute judgment on my persecutors?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 The arrogant have dug pits for me in violation of Your law.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 All Your commandments are faithful; I am persecuted without cause—help me!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 They almost wiped me from the earth, but I have not forsaken Your precepts.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Revive me according to Your loving devotion, that I may obey the testimony of Your mouth.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Your word, O LORD, is everlasting; it is firmly fixed in the heavens.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Your faithfulness continues through all generations; You established the earth, and it endures.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Your ordinances stand to this day, for all things are servants to You.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 If Your law had not been my delight, then I would have perished in my affliction.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 I will never forget Your precepts, for by them You have revived me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 I am Yours; save me, for I have sought Your precepts.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 The wicked wait to destroy me, but I will ponder Your testimonies.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 I have seen a limit to all perfection, but Your commandment is without limit.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Oh, how I love Your law! All day long it is my (meditation)
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Your commandments make me wiser than my enemies, for they are always with me.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 I have more insight than all my teachers, for Your testimonies are my (meditation)
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 I discern more than the elders, for I obey Your precepts.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 I have kept my feet from every evil path, that I may keep Your word.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 I have not departed from Your ordinances, for You Yourself have taught me.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 How sweet are Your words to my taste— sweeter than honey in my mouth!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 I gain understanding from Your precepts; therefore I hate every false way.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Your word is a lamp to my feet and a light to my path.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I have sworn and confirmed that I will keep Your righteous judgments.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I am severely afflicted, O LORD; revive me through Your word.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Accept the freewill offerings of my mouth, O LORD, and teach me Your judgments.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 I constantly take my life in my hands, yet I do not forget Your law.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 The wicked have set a snare for me, but I have not strayed from Your precepts.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Your testimonies are my heritage forever, for they are the joy of my heart.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 I have inclined my heart to perform Your statutes, even to the very end.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 The double-minded I despise, but Your law I love.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 You are my hiding place and my shield; I put my hope in Your word.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Depart from me, you evildoers, that I may obey the commandments of my God.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Sustain me as You promised, that I may live; let me not be ashamed of my hope.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Uphold me, and I will be saved, that I may always regard Your statutes.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 You reject all who stray from Your statutes, for their deceitfulness is in vain.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 All the wicked on earth You discard like dross; therefore I love Your testimonies.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 My flesh trembles in awe of You; I stand in fear of Your judgments.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 I have done what is just and right; do not leave me to my oppressors.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Ensure Your servant’s well-being; do not let the arrogant oppress me.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 My eyes fail, looking for Your salvation, and for Your righteous promise.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Deal with Your servant according to Your loving devotion, and teach me Your statutes.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 I am Your servant; give me understanding, that I may know Your testimonies.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 It is time for the LORD to act, for they have broken Your law.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Therefore I love Your commandments more than gold, even the purest gold.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Therefore I admire all Your precepts and hate every false way.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Wonderful are Your testimonies; therefore I obey them.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 The unfolding of Your words gives light; it informs the simple.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 I open my mouth and pant, longing for Your commandments.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Turn to me and show me mercy, as You do to those who love Your name.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Order my steps in Your word; let no sin rule over me.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Redeem me from the oppression of man, that I may keep Your precepts.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Make Your face shine upon Your servant, and teach me Your statutes.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 My eyes shed streams of tears because Your law is not obeyed.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Righteous are You, O LORD, and upright are Your judgments.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 The testimonies You have laid down are righteous and altogether faithful.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 My zeal has consumed me because my foes forget Your words.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Your promise is completely pure; therefore Your servant loves it.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 I am lowly and despised, but I do not forget Your precepts.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Your righteousness is everlasting and Your law is true.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Trouble and distress have found me, but Your commandments are my delight.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Your testimonies are righteous forever. Give me understanding, that I may live.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 I call with all my heart; answer me, O LORD! I will obey Your statutes.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 I call to You; save me, that I may keep Your testimonies.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 I rise before dawn and cry for help; in Your word I have put my hope.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 My eyes anticipate the watches of night, that I may meditate on Your word.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Hear my voice, O LORD, according to Your loving devotion; give me life according to Your justice.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Those who follow after wickedness draw near; they are far from Your law.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 You are near, O LORD, and all Your commandments are true.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Long ago I learned from Your testimonies that You have established them forever.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Look upon my affliction and rescue me, for I have not forgotten Your law.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Defend my cause and redeem me; revive me according to Your word.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Salvation is far from the wicked because they do not seek Your statutes.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Great are Your mercies, O LORD; revive me according to Your ordinances.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Though my persecutors and foes are many, I have not turned from Your testimonies.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I look on the faithless with loathing because they do not keep Your word.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Consider how I love Your precepts, O LORD; give me life according to Your loving devotion.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 The entirety of Your word is truth, and all Your righteous judgments endure forever.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Rulers persecute me without cause, but my heart fears only Your word.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 I rejoice in Your promise like one who finds great spoil.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 I hate and abhor falsehood, but Your law I love.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seven times a day I praise You for Your righteous judgments.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Abundant peace belongs to those who love Your instruction; nothing can make them stumble.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 I wait for Your salvation, O LORD, and I carry out Your commandments.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 I obey Your testimonies and love them greatly.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I obey Your precepts and Your testimonies, for all my ways are before You.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 May my cry come before You, O LORD; give me understanding according to Your word.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 May my plea come before You; rescue me according to Your promise.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 My lips pour forth praise, for You teach me Your statutes.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 My tongue sings of Your word, for all Your commandments are righteous.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 May Your hand be ready to help me, for I have chosen Your precepts.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 I long for Your salvation, O LORD, and Your law is my delight.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Let me live to praise You; may Your judgments sustain me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I have strayed like a lost sheep; seek Your servant, for I have not forgotten Your commandments.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >