< Numbers 33 >

1 These are the journeys of the Israelites when they came out of the land of Egypt by their divisions under the leadership of Moses and Aaron.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 At the LORD’s command, Moses recorded the stages of their journey. These are the stages listed by their starting points:
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 On the fifteenth day of the first month, on the day after the Passover, the Israelites set out from Rameses. They marched out defiantly in full view of all the Egyptians,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 who were burying all their firstborn, whom the LORD had struck down among them; for the LORD had executed judgment against their gods.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 The Israelites set out from Rameses and camped at Succoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 They set out from Succoth and camped at Etham, on the edge of the wilderness.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 They set out from Etham and turned back to Pi-hahiroth, opposite Baal-zephon, and they camped near Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 They set out from Pi-hahiroth and crossed through the sea, into the wilderness, and they journeyed three days into the Wilderness of Etham and camped at Marah.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 They set out from Marah and came to Elim, where there were twelve springs and seventy palm trees, and they camped there.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 They set out from Elim and camped by the Red Sea.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 They set out from the Red Sea and camped in the Desert of Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 They set out from the Desert of Sin and camped at Dophkah.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 They set out from Dophkah and camped at Alush.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 They set out from Alush and camped at Rephidim, where there was no water for the people to drink.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 They set out from Rephidim and camped in the Wilderness of Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 They set out from the Wilderness of Sinai and camped at Kibroth-hattaavah.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 They set out from Kibroth-hattaavah and camped at Hazeroth.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 They set out from Hazeroth and camped at Rithmah.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 They set out from Rithmah and camped at Rimmon-perez.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 They set out from Rimmon-perez and camped at Libnah.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 They set out from Libnah and camped at Rissah.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 They set out from Rissah and camped at Kehelathah.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 They set out from Kehelathah and camped at Mount Shepher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 They set out from Mount Shepher and camped at Haradah.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 They set out from Haradah and camped at Makheloth.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 They set out from Makheloth and camped at Tahath.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 They set out from Tahath and camped at Terah.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 They set out from Terah and camped at Mithkah.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 They set out from Mithkah and camped at Hashmonah.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 They set out from Hashmonah and camped at Moseroth.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 They set out from Moseroth and camped at Bene-jaakan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 They set out from Bene-jaakan and camped at Hor-haggidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 They set out from Hor-haggidgad and camped at Jotbathah.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 They set out from Jotbathah and camped at Abronah.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 They set out from Abronah and camped at Ezion-geber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 They set out from Ezion-geber and camped at Kadesh in the Wilderness of Zin.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 They set out from Kadesh and camped at Mount Hor, on the outskirts of the land of Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 At the LORD’s command, Aaron the priest climbed Mount Hor and died there on the first day of the fifth month, in the fortieth year after the Israelites had come out of the land of Egypt.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aaron was 123 years old when he died on Mount Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Now the Canaanite king of Arad, who lived in the Negev in the land of Canaan, heard that the Israelites were coming.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 And the Israelites set out from Mount Hor and camped at Zalmonah.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 They set out from Zalmonah and camped at Punon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 They set out from Punon and camped at Oboth.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 They set out from Oboth and camped at Iye-abarim on the border of Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 They set out from Iyim and camped at Dibon-gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 They set out from Dibon-gad and camped at Almon-diblathaim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 They set out from Almon-diblathaim and camped in the mountains of Abarim facing Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 They set out from the mountains of Abarim and camped on the plains of Moab by the Jordan across from Jericho.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 And there on the plains of Moab they camped by the Jordan, from Beth-jeshimoth to Abel-shittim.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 On the plains of Moab by the Jordan across from Jericho, the LORD said to Moses,
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 “Speak to the Israelites and tell them: When you cross the Jordan into the land of Canaan,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 you must drive out before you all the inhabitants of the land, destroy all their carved images and cast idols, and demolish all their high places.
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 You are to take possession of the land and settle in it, for I have given you the land to possess.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 And you are to divide the land by lot according to your clans. Give a larger inheritance to a larger clan and a smaller inheritance to a smaller one. Whatever falls to each one by lot will be his. You will receive an inheritance according to the tribes of your fathers.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 But if you do not drive out the inhabitants of the land before you, those you allow to remain will become barbs in your eyes and thorns in your sides; they will harass you in the land where you settle.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 And then I will do to you what I had planned to do to them.”
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Numbers 33 >