< Job 7 >

1 “Is not man consigned to labor on earth? Are not his days like those of a hired hand?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Like a slave he longs for shade; like a hireling he waits for his wages.
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 So I am allotted months of futility, and nights of misery are appointed me.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 When I lie down I think: ‘When will I get up?’ But the night drags on, and I toss and turn until dawn.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 My flesh is clothed with worms and encrusted with dirt; my skin is cracked and festering.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 My days are swifter than a weaver’s shuttle; they come to an end without hope.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Remember that my life is but a breath. My eyes will never again see happiness.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 The eye that beholds me will no longer see me. You will look for me, but I will be no more.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 As a cloud vanishes and is gone, so he who goes down to Sheol does not come back up. (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 He never returns to his house; his place remembers him no more.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Therefore I will not restrain my mouth; I will speak in the anguish of my spirit; I will complain in the bitterness of my soul.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Am I the sea, or the monster of the deep, that You must keep me under guard?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 When I think my bed will comfort me and my couch will ease my complaint,
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 then You frighten me with dreams and terrify me with visions,
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 so that I would prefer strangling and death over my life in this body.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 I loathe my life! I would not live forever. Leave me alone, for my days are but a breath.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 What is man that You should exalt him, that You should set Your heart upon him,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 that You attend to him every morning, and test him every moment?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Will You never look away from me, or leave me alone to swallow my spittle?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 If I have sinned, what have I done to You, O watcher of mankind? Why have You made me Your target, so that I am a burden to You?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Why do You not pardon my transgression and take away my iniquity? For soon I will lie down in the dust; You will seek me, but I will be no more.”
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >