< Job 34 >

1 Then Elihu continued:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 “Hear my words, O wise men; give ear to me, O men of learning.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 For the ear tests words as the mouth tastes food.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Let us choose for ourselves what is right; let us learn together what is good.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 For Job has declared, ‘I am righteous, yet God has deprived me of justice.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Would I lie about my case? My wound is incurable, though I am without transgression.’
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 What man is like Job, who drinks up derision like water?
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 He keeps company with evildoers and walks with wicked men.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 For he has said, ‘It profits a man nothing that he should delight in God.’
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Therefore listen to me, O men of understanding. Far be it from God to do wrong, and from the Almighty to act unjustly.
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 For according to a man’s deeds He repays him; according to a man’s ways He brings consequences.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Indeed, it is true that God does not act wickedly, and the Almighty does not pervert justice.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Who gave Him charge over the earth? Who appointed Him over the whole world?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 If He were to set His heart to it and withdraw His Spirit and breath,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 all flesh would perish together and mankind would return to the dust.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 If you have understanding, hear this; listen to my words.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Could one who hates justice govern? Will you condemn the just and mighty One,
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 who says to kings, ‘You are worthless!’ and to nobles, ‘You are wicked,’
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 who is not partial to princes and does not favor rich over poor? For they are all the work of His hands.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 They die in an instant, in the middle of the night. The people convulse and pass away; the mighty are removed without human hand.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 For His eyes are on the ways of a man, and He sees his every step.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 There is no darkness or deep shadow where the workers of iniquity can hide.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 For God need not examine a man further or have him approach for judgment.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 He shatters the mighty without inquiry and sets up others in their place.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Therefore, He recognizes their deeds; He overthrows them in the night and they are crushed.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 He strikes them for their wickedness in full view,
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 because they turned aside from Him and had no regard for any of His ways.
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 They caused the cry of the poor to come before Him, and He heard the outcry of the afflicted.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 But when He remains silent, who can condemn Him? When He hides His face, who can see Him? Yet He watches over both man and nation,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 that godless men should not rule or lay snares for the people.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Suppose someone says to God, ‘I have endured my punishment; I will offend no more.
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Teach me what I cannot see; if I have done wrong, I will not do it again.’
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Should God repay you on your own terms when you have disavowed His? You must choose, not I; so tell me what you know.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Men of understanding will declare to me, and the wise men who hear me will say:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 ‘Job speaks without knowledge; his words lack insight.’
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 If only Job were tried to the utmost for answering like a wicked man.
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 For he adds rebellion to his sin; he claps his hands among us and multiplies his words against God.”
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >