< Psalms 115 >

1 Not unto us, O Jehovah, not unto us, But unto thy name give glory, For thy lovingkindness, and for thy truth’s sake.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Wherefore should the nations say, Where is now their God?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 But our God is in the heavens: He hath done whatsoever he pleased.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Their idols are silver and gold, The work of men’s hands.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 They have mouths, but they speak not; Eyes have they, but they see not;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 They have ears, but they hear not; Noses have they, but they smell not;
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 They have hands, but they handle not; Feet have they, but they walk not; Neither speak they through their throat.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 They that make them shall be like unto them; Yea, every one that trusteth in them.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 O Israel, trust thou in Jehovah: He is their help and their shield.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 O house of Aaron, trust ye in Jehovah: He is their help and their shield.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Ye that fear Jehovah, trust in Jehovah: He is their help and their shield.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Jehovah hath been mindful of us; he will bless [us]: He will bless the house of Israel; He will bless the house of Aaron.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 He will bless them that fear Jehovah, Both small and great.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Jehovah increase you more and more, You and your children.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Blessed are ye of Jehovah, Who made heaven and earth.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 The heavens are the heavens of Jehovah; But the earth hath he given to the children of men.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 The dead praise not Jehovah, Neither any that go down into silence;
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 But we will bless Jehovah From this time forth and for evermore. Praise ye Jehovah.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Psalms 115 >