< Proverbs 17 >

1 Better is a dry morsel, and quietness therewith, Than a house full of feasting with strife.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 A servant that dealeth wisely shall have rule over a son that causeth shame, And shall have part in the inheritance among the brethren.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 The refining pot is for silver, and the furnace for gold; But Jehovah trieth the hearts.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 An evil-doer giveth heed to wicked lips; [And] a liar giveth ear to a mischievous tongue.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Whoso mocketh the poor reproacheth his Maker; [And] he that is glad at calamity shall not be unpunished.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Children’s children are the crown of old men; And the glory of children are their fathers.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Excellent speech becometh not a fool; Much less do lying lips a prince.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 A bribe is [as] a precious stone in the eyes of him that hath it; Whithersoever it turneth, it prospereth.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 He that covereth a transgression seeketh love; But he that harpeth on a matter separateth chief friends.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 A rebuke entereth deeper into one that hath understanding Than a hundred stripes into a fool.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 An evil man seeketh only rebellion; Therefore a cruel messenger shall be sent against him.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Let a bear robbed of her whelps meet a man, Rather than a fool in his folly.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Whoso rewardeth evil for good, Evil shall not depart from his house.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 The beginning of strife is [as] when one letteth out water: Therefore leave off contention, before there is quarrelling.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 He that justifieth the wicked, and he that condemneth the righteous, Both of them alike are an abomination to Jehovah.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Wherefore is there a price in the hand of a fool to buy wisdom, Seeing he hath no understanding?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 A friend loveth at all times; And a brother is born for adversity.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 A man void of understanding striketh hands, And becometh surety in the presence of his neighbor.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 He loveth transgression that loveth strife: He that raiseth high his gate seeketh destruction.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 He that hath a wayward heart findeth no good; And he that hath a perverse tongue falleth into mischief.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 He that begetteth a fool [doeth it] to his sorrow; And the father of a fool hath no joy.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 A cheerful heart is a good medicine; But a broken spirit drieth up the bones.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 A wicked man receiveth a bribe out of the bosom, To pervert the ways of justice.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Wisdom is before the face of him that hath understanding; But the eyes of a fool are in the ends of the earth.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 A foolish son is a grief to his father, And bitterness to her that bare him.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Also to punish the righteous is not good, [Nor] to smite the noble for [their] uprightness.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 He that spareth his words hath knowledge; And he that is of a cool spirit is a man of understanding.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Even a fool, when he holdeth his peace, is counted wise; When he shutteth his lips, he is [esteemed as] prudent.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Proverbs 17 >