< Job 21 >

1 Then Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hear diligently my speech; And let this be your consolations.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Suffer me, and I also will speak; And after that I have spoken, mock on.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 As for me, is my complaint to man? And why should I not be impatient?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Mark me, and be astonished, And lay your hand upon your mouth.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Even when I remember I am troubled, And horror taketh hold on my flesh.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Wherefore do the wicked live, Become old, yea, wax mighty in power?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their seed is established with them in their sight, And their offspring before their eyes.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Their houses are safe from fear, Neither is the rod of God upon them.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Their bull gendereth, and faileth not; Their cow calveth, and casteth not her calf.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send forth their little ones like a flock, And their children dance.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They sing to the timbrel and harp, And rejoice at the sound of the pipe.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They spend their days in prosperity, And in a moment they go down to Sheol. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 And they say unto God, Depart from us; For we desire not the knowledge of thy ways.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 What is the Almighty, that we should serve him? And what profit should we have, if we pray unto him?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Lo, their prosperity is not in their hand: The counsel of the wicked is far from me.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How oft is it that the lamp of the wicked is put out? That their calamity cometh upon them? That [God] distributeth sorrows in his anger?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 That they are as stubble before the wind, And as chaff that the storm carrieth away?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 [Ye say], God layeth up his iniquity for his children. Let him recompense it unto himself, that he may know it:
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Let his own eyes see his destruction, And let him drink of the wrath of the Almighty.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For what careth he for his house after him, When the number of his months is cut off?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Shall any teach God knowledge, Seeing he judgeth those that are high?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 One dieth in his full strength, Being wholly at ease and quiet:
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 His pails are full of milk, And the marrow of his bones is moistened.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 And another dieth in bitterness of soul, And never tasteth of good.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 They lie down alike in the dust, And the worm covereth them.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Behold, I know your thoughts, And the devices wherewith ye would wrong me.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye say, Where is the house of the prince? And where is the tent wherein the wicked dwelt?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Have ye not asked wayfaring men? And do ye not know their evidences,
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 That the evil man is reserved to the day of calamity? That they are led forth to the day of wrath?
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who shall declare his way to his face? And who shall repay him what he hath done?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Yet shall he be borne to the grave, And men shall keep watch over the tomb.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 The clods of the valley shall be sweet unto him, And all men shall draw after him, As there were innumerable before him.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 How then comfort ye me in vain, Seeing in your answers there remaineth [only] falsehood?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >