< Genesis 11 >

1 And the whole earth was of one language and of one speech.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 And it came to pass, as they journeyed east, that they found a plain in the land of Shinar; and they dwelt there.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 And they said one to another, Come, let us make brick, and burn them thoroughly. And they had brick for stone, and slime had they for mortar.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 And they said, Come, let us build us a city, and a tower, whose top [may reach] unto heaven, and let us make us a name; lest we be scattered abroad upon the face of the whole earth.
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 And Jehovah came down to see the city and the tower, which the children of men builded.
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 And Jehovah said, Behold, they are one people, and they have all one language; and this is what they begin to do: and now nothing will be withholden from them, which they purpose to do.
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 Come, let us go down, and there confound their language, that they may not understand one another’s speech.
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 So Jehovah scattered them abroad from thence upon the face of all the earth: and they left off building the city.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 Therefore was the name of it called Babel; because Jehovah did there confound the language of all the earth: and from thence did Jehovah scatter them abroad upon the face of all the earth.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 These are the generations of Shem. Shem was a hundred years old, and begat Arpachshad two years after the flood:
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 and Shem lived after he begat Arpachshad five hundred years, and begat sons and daughters.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 And Arpachshad lived five and thirty years, and begat Shelah:
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 and Arpachshad lived after he begat Shelah four hundred and three years, and begat sons and daughters.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 And Shelah lived thirty years, and begat Eber:
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 and Shelah lived after he begat Eber four hundred and three years, and begat sons and daughters.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 And Eber lived four and thirty years, and begat Peleg:
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 and Eber lived after he begat Peleg four hundred and thirty years, and begat sons and daughters.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 And Peleg lived thirty years, and begat Reu:
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 and Peleg lived after he begat Reu two hundred and nine years, and begat sons and daughters.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 And Reu lived two and thirty years, and begat Serug:
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 and Reu lived after he begat Serug two hundred and seven years, and begat sons and daughters.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 And Serug lived thirty years, and begat Nahor:
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 and Serug lived after he begat Nahor two hundred years, and begat sons and daughters.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 And Nahor lived nine and twenty years, and begat Terah:
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 and Nahor lived after he begat Terah a hundred and nineteen years, and begat sons and daughters.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 And Terah lived seventy years, and begat Abram, Nahor, and Haran.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Now these are the generations of Terah. Terah begat Abram, Nahor, and Haran; and Haran begat Lot.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 And Haran died before his father Terah in the land of his nativity, in Ur of the Chaldees.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 And Abram and Nahor took them wives: the name of Abram’s wife was Sarai; and the name of Nahor’s wife, Milcah, the daughter of Haran, the father of Milcah, and the father of Iscah.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 And Sarai was barren; she had no child.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 And Terah took Abram his son, and Lot the son of Haran, his son’s son, and Sarai his daughter-in-law, his son Abram’s wife; and they went forth with them from Ur of the Chaldees, to go into the land of Canaan; and they came unto Haran, and dwelt there.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 And the days of Terah were two hundred and five years: and Terah died in Haran.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

< Genesis 11 >