< Psalms 4 >
1 For the Chief Musician; on stringed instruments. A Psalm by David. Answer me when I call, God of my righteousness. Give me relief from my distress. Have mercy on me, and hear my prayer.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 You sons of men, how long shall my glory be turned into dishonor? Will you love vanity and seek after falsehood? (Selah)
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 But know that the LORD has set apart for himself him who is godly; The LORD will hear when I call to him.
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Stand in awe, and do not sin. Search your own heart on your bed, and be still. (Selah)
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 Offer the sacrifices of righteousness. Put your trust in the LORD.
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 Many say, “Who will show us any good?” LORD, let the light of your face shine on us.
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 You have put gladness in my heart, more than when their grain and their new wine are increased.
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 In peace I will both lay myself down and sleep, for you alone, LORD, make me live in safety.
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.