< Proverbs 14 >

1 Every wise woman builds her house, but the foolish one tears it down with her own hands.
Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
2 He who walks in his uprightness fears the LORD, but he who is perverse in his ways despises him.
Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
3 The fool’s talk brings a rod to his back, but the lips of the wise protect them.
Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
4 Where no oxen are, the crib is clean, but much increase is by the strength of the ox.
Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
5 A truthful witness will not lie, but a false witness pours out lies.
Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
6 A scoffer seeks wisdom, and does not find it, but knowledge comes easily to a discerning person.
Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
7 Stay away from a foolish man, for you will not find knowledge on his lips.
Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
8 The wisdom of the prudent is to think about his way, but the folly of fools is deceit.
Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
9 Fools mock at making atonement for sins, but among the upright there is good will.
Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
10 The heart knows its own bitterness and joy; he will not share these with a stranger.
Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
11 The house of the wicked will be overthrown, but the tent of the upright will flourish.
Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
12 There is a way which seems right to a man, but in the end it leads to death.
Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
13 Even in laughter the heart may be sorrowful, and mirth may end in heaviness.
Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
14 The unfaithful will be repaid for his own ways; likewise a good man will be rewarded for his ways.
Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
15 A simple man believes everything, but the prudent man carefully considers his ways.
Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
16 A wise man fears and shuns evil, but the fool is hot headed and reckless.
Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
17 He who is quick to become angry will commit folly, and a crafty man is hated.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
18 The simple inherit folly, but the prudent are crowned with knowledge.
Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
19 The evil bow down before the good, and the wicked at the gates of the righteous.
Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
20 The poor person is shunned even by his own neighbor, but the rich person has many friends.
Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
21 He who despises his neighbor sins, but he who has pity on the poor is blessed.
Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
22 Do not they go astray who plot evil? But love and faithfulness belong to those who plan good.
Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
23 In all hard work there is profit, but the talk of the lips leads only to poverty.
Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
24 The crown of the wise is their riches, but the folly of fools crowns them with folly.
Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
25 A truthful witness saves souls, but a false witness is deceitful.
Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
26 In the fear of the LORD is a secure fortress, and he will be a refuge for his children.
Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
27 The fear of the LORD is a fountain of life, turning people from the snares of death.
Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
28 In the multitude of people is the king’s glory, but in the lack of people is the destruction of the prince.
Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
29 He who is slow to anger has great understanding, but he who has a quick temper displays folly.
Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
30 The life of the body is a heart at peace, but envy rots the bones.
Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
31 He who oppresses the poor shows contempt for his Maker, but he who is kind to the needy honors him.
Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
32 The wicked is brought down in his calamity, but in death, the righteous has a refuge.
Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
33 Wisdom rests in the heart of one who has understanding, and is even made known in the inward part of fools.
Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
34 Righteousness exalts a nation, but sin is a disgrace to any people.
Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
35 The king’s favor is toward a servant who deals wisely, but his wrath is toward one who causes shame.
Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

< Proverbs 14 >