< Song of Solomon 7 >

1 How beautiful are thy feet in sandals, O prince's daughter! Thy rounded thighs are like jewels, the work of the hands of a skilful workman.
Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
2 Thy body is a round goblet, no mingled wine is wanting. Thy waist is a heap of wheat set about with lilies.
Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
3 Thy two breasts are like two fawns that are twins of a roe.
Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
4 Thy neck is like the tower of ivory. Thine eyes, the pools in Heshbon, by the gate of Bath-rabbim. Thy nose is like the tower of Lebanon which looks toward Damascus.
Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
5 Thy head upon thee is like Carmel, and the hair of thy head like purple. The king is held captive in the tresses.
Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
6 How fair and how pleasant thou are, O love, for delights!
Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
7 This thy stature is like to a palm tree, and thy breasts to its clusters.
Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
8 I said, I will climb up into the palm tree. I will take hold of the branches of it. Let thy breasts be as clusters of the vine, and the smell of thy breath like apples,
Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
9 and thy mouth like the best wine, that goes down smoothly for my beloved, gliding through the lips and teeth.
ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
10 I am my beloved's, and his desire is toward me.
Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
11 Come, my beloved, let us go forth into the field. Let us lodge in the villages.
Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
12 Let us get up early to the vineyards. Let us see whether the vine has budded, its blossom is open, the pomegranates are in flower. There I will give thee my love.
Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
13 The mandrakes give forth fragrance. And at our doors are all manner of precious fruits, new and old, which I have laid up for thee, O my beloved.
Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

< Song of Solomon 7 >