< Psalms 70 >

1 Hasten, O God, to deliver me. Make haste to help me, O Jehovah.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Let them be put to shame and confounded who seek after my soul. Let them be turned backward and brought to dishonor who delight in my hurt.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 Let them be turned back because of their shame who say, Aha, aha.
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Let all those who seek thee rejoice and be glad in thee. And let such as love thy salvation say continually, Let God be magnified.
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 But I am poor and needy. Make haste to me, O God. Thou are my help and my deliverer, O Jehovah. Delay thou not.
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

< Psalms 70 >