< Job 39 >
1 Do thou know the time when the wild goats of the rock bring forth? Or can thou mark when the hinds do calve?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Can thou number the months that they fulfill? Or do thou know the time when they bring forth?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 They bow themselves. They bring forth their young. They cast out their pains.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Their young ones become strong. They grow up in the open field. They go forth, and return not again.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Who has sent out the wild donkey free? Or who has loosed the bonds of the swift donkey
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 whose home I have made the wilderness, and the salt land his dwelling-place?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 He scorns the tumult of the city, neither does he hear the shoutings of the driver.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 The range of the mountains is his pasture, and he searches after every green thing.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Will the wild-ox be content to serve thee? Or will he abide by thy crib?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Can thou bind the wild-ox with his band in the furrow? Or will he harrow the valleys after thee?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Will thou trust him because his strength is great? Or will thou leave to him thy labor?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Will thou confide in him that he will bring home thy seed, and gather the grain of thy threshing-floor?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 The wings of the ostrich wave proudly, but are they the pinions and plumage of love?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 For she leaves her eggs on the ground, and warms them in the dust.
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 And she forgets that the foot may crush them, or that the wild beast may trample them.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 She deals hardly with her young ones, as if they were not hers. Though her labor be in vain, she is without fear,
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 because God has deprived her of wisdom, nor has he imparted understanding to her.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 The time she lifts up herself on high she scorns the horse and his rider.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Have thou given the horse his might? Have thou clothed his neck with the quivering mane?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Have thou made him to leap as a locust? The glory of his snorting is awesome.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 He paws in the valley, and rejoices in his strength. He goes out to meet the armed men.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 He mocks at fear, and is not dismayed. Neither does he turn back from the sword.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 The quiver rattles against him, the flashing spear and the javelin.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 He swallows the ground with fierceness and rage, nor does he believe that it is the voice of the trumpet.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 As often as the trumpet sounds he says, Aha! And he smells the battle afar off, the thunder of the captains, and the shouting.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Is it by thy wisdom that the hawk soars, and stretches her wings toward the south?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Is it at thy command that the eagle mounts up, and makes her nest on high?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 She dwells on the cliff, and makes her home upon the point of the cliff and the stronghold.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 From there she spies out the prey. Her eyes behold it afar off.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Her young ones also suck up blood. And where the slain are, there is she.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”