< Ezekiel 39 >

1 And thou, son of man, prophesy against Gog, and say, Thus says the lord Jehovah: Behold, I am against thee, O Gog, ruler of Rosh, Meshech, and Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 And I will turn thee about, and will lead thee on, and will cause thee to come up from the outermost parts of the north, and I will bring thee upon the mountains of Israel.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 And I will smite thy bow out of thy left hand, and will cause thine arrows to fall out of thy right hand.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Thou shall fall upon the mountains of Israel, thou, and all thy hordes, and the peoples who are with thee. I will give thee to the ravenous birds of every sort, and to the beasts of the field to be devoured.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Thou shall fall upon the open field, for I have spoken it, says the lord Jehovah.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 And I will send a fire on Magog, and on those who dwell securely in the isles. And they shall know that I am Jehovah.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 And I will make my holy name known in the midst of my people Israel, nor will I allow my holy name to be profaned any more. And the nations shall know that I am Jehovah, the Holy One in Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Behold, it comes, and it shall be done, says the lord Jehovah. This is the day of which I have spoken.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 And those who dwell in the cities of Israel shall go forth, and shall make fires of the weapons and burn them, both the shields and the bucklers, the bows and the arrows, and the hand staves, and the spears. And they shall make fires of them seven years,
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 so that they shall take no wood out of the field, nor cut down any out of the forests, for they shall make fires of the weapons. And they shall plunder those who plundered them, and rob those who robbed them, says the lord Jehovah.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 And it shall come to pass in that day, that I will give to Gog a place for burial in Israel: the valley of those who pass through on the east of the sea. And it shall stop those who pass through, and they shall bury Gog and all his multitude there. And they shall call it The valley of Hamon-gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 And the house of Israel shall be burying them seven months, that they may cleanse the land.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Yea, all the people of the land shall bury them, and it shall be to them a renown in the day that I shall be glorified, says the lord Jehovah.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 And they shall set apart men of continual employment, who shall pass through the land. And, with those who pass through, those that bury those who remain upon the face of the land, to cleanse it, after the end of seven months they shall search.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 And those who pass through the land shall pass through, and when any man sees a man's bone, then he shall set up a sign by it till the buriers have buried it in the valley of Hamon-gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 And Hamonah shall also be the name of a city. Thus they shall cleanse the land.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 And thou, son of man, thus says the lord Jehovah: Speak to the birds of every sort, and to every beast of the field, Assemble yourselves, and come. Gather yourselves on every side to my sacrifice that I sacrifice for you, even a great sacrifice upon the mountains of Israel, that ye may eat flesh and drink blood.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Ye shall eat the flesh of the mighty, and drink the blood of the rulers of the earth, of rams, of lambs, and of goats, of bullocks, all of them fatlings of Bashan.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 And ye shall eat fat till ye be full, and drink blood till ye be drunken, of my sacrifice which I have sacrificed for you.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 And ye shall be filled at my table with horses and chariots, with mighty men, and with all men of war, says the lord Jehovah.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 And I will set my glory among the nations. And all the nations shall see my judgment that I have executed, and my hand that I have laid upon them.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 So the house of Israel shall know that I am Jehovah their God, from that day and forward.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 And the nations shall know that the house of Israel went into captivity for their iniquity, because they trespassed against me, and I hid my face from them. So I gave them into the hand of their adversaries, and they fell all of them by the sword.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 I did to them according to their uncleanness and according to their transgressions. And I hid my face from them.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Therefore thus says the lord Jehovah: Now I will bring back the captivity of Jacob, and have mercy upon the whole house of Israel. And I will be jealous for my holy name.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 And they shall bear their shame, and all their trespasses by which they have trespassed against me, when they shall dwell securely in their land. And none shall make them afraid
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 when I have brought them back from the peoples, and gathered them out of their enemies' lands, and am sanctified in them in the sight of many nations.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 And they shall know that I am Jehovah their God, in that I caused them to go into captivity among the nations, and have gathered them to their own land. And I will leave none of them any more there,
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 nor will I hide my face any more from them. For I have poured out my Spirit upon the house of Israel, says the lord Jehovah.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 39 >