< Acts 20 >
1 And after the uproar ceased, Paul having summoned the disciples and having embraced them, he departed to go into Macedonia.
Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
2 And having passed through those parts, and having exhorted them with many words, he came into Greece.
Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
3 And having spent three months there, and a conspiracy having developed against him by Jews, intending to go up into Syria, a decision developed to return through Macedonia.
Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
4 And there accompanied him as far as Asia, Sopater a Berean, and of the Thessalonians, Aristarchus and Secundus, and Gaius a Derbean, and Timothy, and the Asians, Tychicus and Trophimus.
Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
5 These men, who went ahead, awaited us at Troas.
Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
6 And we sailed away from Philippi after the days of unleavened bread, and came to them at Troas within five days, where we stayed seven days.
Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
7 And upon the first day of the week, the disciples having come together to break bread, Paul discoursed with them, intending to depart on the morrow. And he prolonged his speech until midnight.
Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
8 And there were considerable lights in the upper floor where we were gathered together.
Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
9 And a certain young man named Eutychus sitting in the window, being carried away by deep sleep (Paul discoursing on more), being carried away by sleep, he fell down below from the third floor, and was taken up dead.
Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
10 But Paul having come down, he fell on him, and having embraced him he said, Be not troubled, for his life is in him.
Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
11 And after getting up, and having broken bread and eaten, and having conversed for a considerable time, until dawn, thus he departed.
Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
12 And they brought the boy alive, and were not a little comforted.
Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
13 But we, having gone ahead to the ship, went up to Assos, intending from there to take up Paul, for so it was arranged, he himself intending to go on foot.
Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
14 And when he met with us at Assos, having taken him up, we came to Mitylene.
Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
15 And having sailed from there on the next day, we arrived opposite Chios, and the next day we came near to Samos. And having remained in Trogyllium, on the following day we came to Miletus.
Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
16 For Paul determined to sail past Ephesus, so that he might not happen to lose time in Asia. For he was hastening, if it were possible, for him to become at Jerusalem the day of Pentecost.
Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
17 And from Miletus having sent to Ephesus, he summoned the elders of the congregation.
Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
18 And when they came to him, he said to them, Ye know, from the first day in which I stepped in Asia, how I became with you all the time,
Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
19 serving the Lord with all humility, and many tears and trials that befell me by the conspiracies of the Jews.
Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
20 How I kept back nothing of these things that are beneficial, not to inform you, and to teach you in public, and from house to house,
Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
21 testifying both to Jews and to Greeks repentance toward God, and faith toward our Lord Jesus.
Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
22 And now behold, I, bound in the spirit, am going to Jerusalem, not knowing the things that will happen to me in it,
“Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
23 except that the Holy Spirit testifies from city to city, saying that bonds and afflictions await me.
Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
24 But I make nothing of the matter, nor do I hold my life precious to myself, so as to fully complete my course with joy, and the ministry that I received from the Lord Jesus, to solemnly testify the good news of the grace of God.
Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
25 And now behold, I have seen that ye will no longer see my face, ye all among whom I passed through preaching the kingdom of God.
“Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
26 Therefore I solemnly declare to you this day, that I am clean from the blood of all men.
Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
27 For I did not withdraw from declaring to you the whole plan of God.
Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
28 Take heed therefore to yourselves, and to all the flock, among which the Holy Spirit placed you guardians, to tend the church of the Lord and God, which he purchased by his own blood.
Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
29 For I know this, that after my departure grievous wolves will enter in among you, not sparing the flock.
Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
30 And from you yourselves men will rise up, speaking distorted things, to draw away the disciples after them.
Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
31 Therefore watch ye, remembering that for three years, night and day, I did not cease warning each one with tears.
Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
32 And now brothers, I commit you to God, and to the word of his grace, which is able to build up, and to give you an inheritance among all those who have been sanctified.
“Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
33 I coveted no man's silver, or gold, or apparel.
Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
34 Ye yourselves know that these hands served my needs, and to those who were with me.
Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
35 I gave you a glimpse of all things, that so laboring ye ought to aid the weak, and to remember the words of the Lord Jesus, that he himself said, It is more blessed to give than to receive.
Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
36 And having spoken these things, having knelt down, he prayed with them all.
Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
37 And there developed considerable weeping of all. And having fallen on Paul's neck, they kissed him much,
Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
38 sorrowing especially for the word that he had spoken, that they were going to see his face no more. And they accompanied him to the ship.
Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.