< 2 Thessalonians 2 >

1 Now we ask you, brothers, on behalf of the coming of our Lord Jesus Christ and our gathering together to him,
Pa za kubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikumane naye, abale, tikukupemphani
2 for ye not to be quickly shaken from your mind, nor to be alarmed, neither by spirit, nor by word, nor by a letter as by us, as that the day of the Christ has come.
kuti musagwedezeke msanga mʼmaganizo kapena kuopsezedwa ndi uneneri, mbiri kapena kalata yokhala ngati yachokera kwa ife, yonena kuti tsiku lija la Ambuye linafika kale.
3 Let not any man deceive you in any way, because if not, the defection may come first, and he may be revealed-the man of sin, the son of destruction,
Musalole kuti wina aliyense akunamizeni mwa njira ina iliyonse. Pakuti tsikulo lisanafike, kudzakhala mpatuko waukulu kwambiri, ndipo kudzaoneka munthu woyipitsitsa uja, munthu woyenera kuwonongedwayo.
4 who opposes and exalts himself against all that is called God or an object of worship, so as for him to sit in the temple of God, as God, displaying himself that he is God.
Iyeyo adzatsutsa ndi kudziyika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza. Iyeyo adzadzikhazika mʼNyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.
5 Do ye not remember that when I was yet with you I told you these things?
Kodi simukukumbukira kuti pamene ndinali nanu pamodzi ndinkakuwuzani zimenezi?
6 And now ye know that which restrains, for him to be revealed in his own time.
Ndipo tsopano mukudziwa chimene chikumuletsa kuonekera, koma adzawululika pa nthawi yake yoyenera.
7 For the mystery of lawlessness is already working, only he who restrains it until now will develop from the midst.
Pakuti mphamvu yobisika yoyipitsitsa ikugwira ntchito ngakhale tsopano; koma amene akutchinga mphamvuyo adzapitiriza kutero mpaka pamene wotchingayo adzachotsedwe.
8 And then the lawless will be revealed, whom the Lord will consume with the spirit of his mouth, and will neutralize at the appearance of his coming.
Ndipo kenaka woyipitsitsayo adzaonekera, amene Ambuye Yesu adzamugonjetsa ndi mpweya otuluka mʼkamwa mwake ndi kumuwononga ndi ulemerero wa kubwera kwake.
9 Whose coming is according to the working of Satan with all power and signs and marvels of deceit,
Woyipitsitsayo adzabwera ndi mphamvu za Satana. Adzaonetsa mphamvu zake pochita zizindikiro ndi zodabwitsa zachinyengo.
10 and in all deception of unrighteousness in those who are perishing, in return for which, they did not accept the love of the truth in order for them to be saved.
Iye adzagwiritsa ntchito mtundu uliwonse wachinyengo kupusitsa amene akuwonongeka. Iwo akuwonongeka chifukwa akukana kukonda choonadi ndi kuti apulumutsidwe.
11 And because of this God will send them the force of a delusion, for them to believe a lie,
Chifukwa cha chimenechi, Mulungu akuwatumizira chinyengo chachikulu kuti akhulupirire bodza.
12 so that they might be condemned-all those who did not believe the truth, but who delighted in unrighteousness.
Choncho adzalangidwa onse amene sanakhulupirire choonadi, koma anakondwera mu zoyipa.
13 But we are indebted to express thanks to God always about you, brothers, beloved by the Lord, because God chose you from the beginning for salvation, in sanctification of spirit and belief of truth,
Koma tiyenera kuyamika Mulungu chifukwa cha inu abale okondedwa mwa Ambuye, pakuti Mulungu anakusankhani pachiyambi pomwe kuti mupulumuke chifukwa cha ntchito yoyeretsa ya Mzimu ndi chikhulupiriro chanu mʼchoonadi.
14 for which he called you, through our good news, for an acquired possession of glory of our Lord Jesus Christ.
Iye anakuyitanirani zimenezi kudzera mwa uthenga wathu wabwino, kuti mulandire nawo ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu.
15 So then, brothers, stand firm and hold to the traditions that ye were taught, whether by word or by letter from us.
Kotero tsono, abale, imani mwamphamvu ndi kugwiritsa ziphunzitso zimene tinakupatsani kudzera mʼmawu apakamwa kapena kudzera mʼkalata.
16 And may our Lord Jesus Christ himself, and our God and Father who loved us and gave eternal encouragement and good hope through grace, (aiōnios g166)
Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, (aiōnios g166)
17 encourage your hearts and establish you in every good word and work.
akulimbikitseni ndi kukupatsani mphamvu yogwirira ntchito ndi kuyankhula zabwino zilizonse.

< 2 Thessalonians 2 >