< 1 Samuel 8 >
1 And it came to pass, when Samuel was old, that he made his sons judges over Israel.
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 Now the name of his firstborn was Joel, and the name of his second, Abijah. They were judges in Beersheba.
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 And his sons did not walk in his ways, but turned aside after dishonest gain, and took bribes, and perverted justice.
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 Then all the elders of Israel gathered themselves together, and came to Samuel to Ramah.
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 And they said to him, Behold, thou are old, and thy sons do not walk in thy ways. Now make for us a king to judge us like all the nations.
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 But the thing displeased Samuel when they said, Give us a king to judge us. And Samuel prayed to Jehovah.
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 And Jehovah said to Samuel, Hearken to the voice of the people in all that they say to thee, for they have not rejected thee, but they have rejected me, that I should not be king over them.
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 According to all the works which they have done since the day that I brought them up out of Egypt even to this day, in that they have forsaken me, and served other gods, so do they also to thee.
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 Now therefore hearken to their voice. However thou shall protest solemnly to them, and shall show them the manner of the king who shall reign over them.
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 And Samuel told all the words of Jehovah to the people who asked of him a king.
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 And he said, This will be the manner of the king who shall reign over you: He will take your sons, and appoint them to him for his chariots, and to be his horsemen, and they shall run before his chariots.
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 And he will appoint them to him for captains of thousands, and captains of fifties. And he will set some to plow his ground, and to reap his harvest, and to make his instruments of war, and the instruments of his chariots.
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 And he will take your daughters to be perfumers, and to be cooks, and to be bakers.
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 And he will take your fields, and your vineyards, and your oliveyards, even the best of them, and give them to his servants.
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 And he will take the tenth of your seed, and of your vineyards, and give to his officers, and to his servants.
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 And he will take your men-servants, and your maid-servants, and your finest young men, and your donkeys, and put them to his work.
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 He will take the tenth of your flocks. And ye shall be his servants.
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 And ye shall cry out in that day because of your king whom ye shall have chosen you, and Jehovah will not answer you in that day.
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 But the people refused to hearken to the voice of Samuel. And they said, No, but we will have a king over us
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 that we also may be like all the nations, and that our king may judge us, and go out before us, and fight our battles.
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 And Samuel heard all the words of the people, and he repeated them in the ears of Jehovah.
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 And Jehovah said to Samuel, Hearken to their voice, and make for them a king. And Samuel said to the men of Israel, Go ye every man to his city.
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”