< 1 Samuel 7 >

1 And the men of Kiriath-jearim came, and fetched up the ark of Jehovah, and brought it into the house of Abinadab in the hill, and sanctified Eleazar his son to keep the ark of Jehovah.
Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
2 And it came to pass, from the day that the ark abode in Kiriath-jearim, that the time was long, for it was twenty years, and all the house of Israel lamented after Jehovah.
Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
3 And Samuel spoke to all the house of Israel, saying, If ye do return to Jehovah with all your heart, then put away the foreign gods and the Ashtaroth from among you, and direct your hearts to Jehovah, and serve him only. And he will deliver you out of the hand of the Philistines.
Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
4 Then the sons of Israel did put away the Baalim and the Ashtaroth, and served Jehovah only.
Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
5 And Samuel said, Gather all Israel to Mizpah, and I will pray for you to Jehovah.
Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
6 And they gathered together to Mizpah, and drew water, and poured it out before Jehovah, and fasted on that day, and said there, We have sinned against Jehovah. And Samuel judged the sons of Israel in Mizpah.
Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
7 And when the Philistines heard that the sons of Israel were gathered together to Mizpah, the lords of the Philistines went up against Israel. And when the sons of Israel heard it, they were afraid of the Philistines.
Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
8 And the sons of Israel said to Samuel, Do not cease to cry to Jehovah our God for us, that he will save us out of the hand of the Philistines.
Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
9 And Samuel took a sucking lamb, and offered it for a whole burnt offering to Jehovah. And Samuel cried to Jehovah for Israel, and Jehovah answered him.
Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
10 And as Samuel was offering up the burnt offering, the Philistines drew near to battle against Israel, but Jehovah thundered with a great thunder on that day upon the Philistines, and discomfited them, and they were smitten down before Israel.
Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
11 And the men of Israel went out of Mizpah, and pursued the Philistines, and smote them until they came under Beth-car.
Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
12 Then Samuel took a stone, and set it between Mizpah and Shen, and called the name of it Ebenezer, saying, Jehovah has helped us to now.
Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
13 So the Philistines were subdued, and they came no more within the border of Israel, and the hand of Jehovah was against the Philistines all the days of Samuel.
Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
14 And the cities which the Philistines had taken from Israel were restored to Israel, from Ekron even to Gath. And Israel delivered the border of it out of the hand of the Philistines. And there was peace between Israel and the Amorites.
Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
15 And Samuel judged Israel all the days of his life.
Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
16 And he went from year to year in circuit to Bethel, and Gilgal, and Mizpah. And he judged Israel in all those places.
Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
17 And his return was to Ramah, for his house was there. And there he judged Israel, and there he built an altar to Jehovah.
Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 7 >