< 1 Peter 5 >
1 I, a fellow elder and witness of the sufferings of the Christ, and a partaker of the glory going be revealed, exhort the elders among you:
Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
2 Tend ye the flock of God among you, watching over, not by obligation, but willingly, nor greedily, but readily,
Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
3 nor as domineering over the lots, but becoming examples of the flock.
Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
4 And when the chief Shepherd is made known, ye will receive the unfading crown of glory.
Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
5 Likewise younger men should be subordinate to the elder men. And all being subordinate to each other, clothe yourselves with humility, because God sets himself against the haughty, but gives grace to the lowly.
Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
6 Therefore be lowered under the mighty hand of God, so that he may lift you up in time,
Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
7 having cast all your concern upon him, because he cares for you.
Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
8 Be sober, be vigilant. Your opponent the devil, as a roaring lion, walks about seeking whom to devour.
Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
9 Whom resist, steadfast in the faith, knowing the same sufferings are to be accomplished in the world by your brotherhood.
Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
10 And may the God of all grace who called you to his eternal glory in Christ Jesus (after suffering a little while) himself thoroughly prepare you. He will establish, strengthen, and provide a foundation. (aiōnios )
Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
11 To him is the glory and the dominion into the ages of the ages. Truly. (aiōn )
Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
12 By Silvanus, the faithful brother to you, as I reckon, I wrote because of a few things, exhorting and testifying this to be the true grace of God in which ye stand.
Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
13 She in Babylon, chosen together, salutes you, and my son Mark.
Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
14 Salute each other by a kiss of love. Peace to you, to all those in Christ Jesus. Truly.
Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.