< Psalmen 33 >

1 Gij rechtvaardigen! zingt vrolijk in den HEERE; lof betaamt den oprechten.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Looft den HEERE met de harp; psalmzingt Hem met de luit, en het tiensnarig instrument.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Zingt Hem een nieuw lied; speelt wel met vrolijk geschal.
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Want des HEEREN woord is recht, en al Zijn werk getrouw.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 Hij heeft gerechtigheid en gericht lief; de aarde is vol van de goedertierenheid des HEEREN.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Door het Woord des HEEREN zijn de hemelen gemaakt, en door den Geest Zijns monds al hun heir.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Hij vergadert de wateren der zee als op een hoop; Hij stelt den afgronden schatkameren.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Laat de ganse aarde voor den HEERE vrezen; laat alle inwoners van de wereld voor Hem schrikken.
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 Want Hij spreekt, en het is er; Hij gebiedt, en het staat er.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 De HEERE vernietigt den raad der heidenen; Hij breekt de gedachten der volken.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 Maar de raad des HEEREN bestaat in eeuwigheid, de gedachten Zijns harten van geslacht tot geslacht.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Welgelukzalig is het volk, welks God de HEERE is; het volk, dat Hij Zich ten erve verkoren heeft.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 De HEERE schouwt uit den hemel, en ziet alle mensenkinderen.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 Hij ziet uit van Zijn vaste woonplaats op alle inwoners der aarde.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Hij formeert hun aller hart; Hij let op al hun werken.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 Een koning wordt niet behouden door een groot heir; een held wordt niet gered door grote kracht;
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Het paard feilt ter overwinning, en bevrijdt niet door zijn grote sterkte.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Ziet, des HEEREN oog is over degenen, die Hem vrezen, op degenen, die op Zijn goedertierenheid hopen.
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 Om hun ziel van den dood te redden, en om hen bij het leven te houden in den honger.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Onze ziel verbeidt den HEERE: Hij is onze Hulp en ons Schild.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Want ons hart is in Hem verblijd, omdat wij op den Naam Zijner heiligheid vertrouwen.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Uw goedertierenheid, HEERE! zij over ons; gelijk als wij op U hopen.
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< Psalmen 33 >