< Psalmen 121 >

1 Een lied Hammaaloth. Ik hef mijn ogen op naar de bergen, van waar mijn hulp komen zal.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Mijn hulp is van den HEERE, Die hemel en aarde gemaakt heeft.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Hij zal uw voet niet laten wankelen; uw Bewaarder zal niet sluimeren.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Ziet, de Bewaarder Israels zal niet sluimeren, noch slapen.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 De HEERE is uw Bewaarder, de HEERE is uw Schaduw, aan uw rechterhand.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 De zon zal u des daags niet steken, noch de maan des nachts.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 De HEERE zal u bewaren van alle kwaad; uw ziel zal Hij bewaren.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 De HEERE zal uw uitgang en uw ingang bewaren, van nu aan tot in der eeuwigheid.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Psalmen 121 >