< Klaagliederen 5 >

1 Gedenk, HEERE, wat ons geschied is, aanschouw het, en zie onzen smaad aan.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Ons erfdeel is tot de vreemdelingen gewend, onze huizen tot de uitlanders.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Wij zijn wezen zonder vader, onze moeders zijn als de weduwen.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Ons water moeten wij voor geld drinken; ons hout komt ons op prijs te staan.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Wij lijden vervolging op onze halzen; zijn wij woede, men laat ons geen rust.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Wij hebben den Egyptenaar de hand gegeven, en den Assyrier, om met brood verzadigd te worden.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Onze vaders hebben gezondigd, en zijn niet meer, en wij dragen hun ongerechtigheden.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Knechten heersen over ons; er is niemand, die ons uit hun hand rukke.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Wij moeten ons brood met gevaar onzes levens halen, vanwege het zwaard der woestijn.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Onze huid is zwart geworden gelijk een oven, vanwege den geweldigen storm des hongers.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Zij hebben de vrouwen te Sion verkracht, en de jonge dochters in de steden van Juda.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 De vorsten zijn door hunlieder hand opgehangen; de aangezichten der ouden zijn niet geeerd geweest.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Zij hebben de jongelingen weggenomen, om te malen, en de jongens struikelen onder het hout.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 De ouden houden op van de poort, de jongelingen van hun snarenspel.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 De vreugde onzes harten houdt op, onze rei is in treurigheid veranderd.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 De kroon onzes hoofds is afgevallen; o wee nu onzer, dat wij zo gezondigd hebben!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Daarom is ons hart mat, om deze dingen zijn onze ogen duister geworden.
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 Om des bergs Sions wil, die verwoest is, waar de vossen op lopen.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Gij, o HEERE, zit in eeuwigheid, Uw troon is van geslacht tot geslacht.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Waarom zoudt Gij ons steeds vergeten? Waarom zoudt Gij ons zo langen tijd verlaten?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 HEERE, bekeer ons tot U, zo zullen wij bekeerd zijn; vernieuw onze dagen als van ouds.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Want zoudt Gij ons ganselijk verwerpen? Zoudt Gij zozeer tegen ons verbolgen zijn?
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Klaagliederen 5 >