< Psalmen 87 >

1 Een psalm, een lied voor de kinderen van Korach. Zijn grondslag is op de bergen der heiligheid.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 De HEERE bemint de poorten van Sion boven alle woningen van Jakob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Zeer heerlijke dingen worden van u gesproken, o stad Gods! (Sela)
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 Ik zal Rahab en Babel vermelden, onder degenen, die Mij kennen; ziet, de Filistijn, en de Tyrier, met den Moor, deze is aldaar geboren.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 En van Sion zal gezegd worden: Die en die is daarin geboren; en de Allerhoogste Zelf zal hen bevestigen.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 De HEERE zal hen rekenen in het opschrijven der volken, zeggende: Deze is aldaar geboren. (Sela)
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 En de zangers, gelijk de speellieden, mitsgaders al mijn fonteinen, zullen binnen u zijn.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

< Psalmen 87 >