< Psalmen 113 >

1 Hallelujah! Looft, gij knechten des HEEREN! looft den Naam des HEEREN.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 De Naam des HEEREN zij geprezen, van nu aan tot in der eeuwigheid.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Van den opgang der zon af tot haar nedergang, zij de Naam des HEEREN geloofd.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 De HEERE is hoog boven alle heidenen, boven de hemelen is Zijn heerlijkheid.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Wie is gelijk de HEERE, onze God? Die zeer hoog woont.
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Die zeer laag ziet, in den hemel en op de aarde.
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Die den geringe uit het stof opricht, en den nooddruftige uit den drek verhoogt;
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 Om te doen zitten bij de prinsen, bij de prinsen Zijns volks.
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 Die de onvruchtbare doet wonen met een huisgezin, een blijde moeder van kinderen. Hallelujah!
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalmen 113 >