< Psalmen 75 >
1 Voor muziekbegeleiding; op de wijze: "Verderf niet." Een psalm van Asaf; een lied. Wij loven U, God, en prijzen U, Wij roepen uw Naam aan, en vermelden uw wonderen!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Als Ik de tijd acht gekomen, Zal Ik een rechtvaardig oordeel houden:
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 Al wankelt de aarde met al haar bewoners, Ik zet haar zuilen weer recht!
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Daarom roep ik de hoogmoedigen toe: Weest niet trots, De goddelozen: Steekt de hoorn niet omhoog!
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Steekt uw hoorn tegen de hemel niet op, En spreekt niet hooghartig tegen de Rots!
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Want niet uit het oosten of westen, Niet uit de woestijn komt de glorie!
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Neen, het is God, die zal richten, Den een vernederen, den ander verheffen!
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Want in Jahweh’s hand is een beker Met schuimende wijn vol bittere kruiden! Hij schenkt hem leeg tot de droesem toe: Alle bozen der aarde moeten slurpen en drinken.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Maar ìk zal in eeuwigheid jubelen, Den God van Jakob mijn loflied zingen:
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Alle hoornen der bozen worden gebroken, Maar de hoornen der rechtvaardigen steken omhoog!
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.