< Psalmen 106 >

1 Halleluja! Looft Jahweh, want Hij is goed En zijn genade duurt eeuwig!
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Wie kan Jahweh’s machtige daden vermelden, En heel zijn glorie verkonden?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Gelukkig hij, die de wet onderhoudt, En altijd het goede blijft doen!
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Wees ons indachtig, o Jahweh, Om uw liefde voor uw volk; Zoek ons op met uw heil,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Opdat wij het geluk uwer vrienden aanschouwen, Met uw blijde volk ons verblijden, Met uw erfdeel mogen roemen!
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Ach, wij hebben gezondigd met onze vaderen, Wij hebben misdreven en kwaad gedaan!
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Onze vaderen in Egypte Hebben al niet op uw wonderen gelet; En zonder aan uw talrijke gunsten te denken, Zich bij de Rode Zee tegen den Allerhoogste verzet!
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Toch redde Hij hen om wille van zijn Naam, En om zijn almacht te tonen:
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Hij bedreigde de Rode Zee, ze liep droog, Hij leidde hen tussen de golven als door een uitgedroogd land.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Hij redde hen uit de hand van hun haters, Verloste hen uit de macht van hun vijand;
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 De wateren spoelden over hun vijanden heen, En geen bleef er over!
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Toen sloegen ze geloof aan zijn woorden, En zongen zijn lof.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Maar spoedig waren ze weer zijn werken vergeten, En wachtten zijn raadsbesluiten niet af;
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Ze gaven zich in de woestijn aan hun gulzigheid over, En stelden God op de proef in de steppe.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Hij schonk hun wat ze Hem vroegen, Maar Hij liet ze er spoedig van walgen.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Daarna werden ze in hun kamp afgunstig op Moses, En op Aäron, aan Jahweh gewijd.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Maar de aarde spleet open, zwolg Datan in, En bedolf de bent van Abiram;
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Vuur verbrandde hun aanhang, Vlammen verteerden de bozen!
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Dan maakten ze een kalf bij de Horeb, En wierpen zich voor een afgietsel neer;
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Ze verruilden hun Glorie Voor het beeld van een grasvretend rund.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Ze vergaten God, hun Verlosser Die grote dingen in Egypte had gedaan,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Wonderwerken in het land van Cham, Ontzaglijke daden bij de Rode Zee.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 En zeker had Hij hun verdelging beslist, Als Moses, zijn geliefde, er niet was geweest; Maar deze stelde zich tegen Hem in de bres, Om Hem te weerhouden, hen in zijn toorn te vernielen.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Later versmaadden ze het heerlijke land, En sloegen geen geloof aan zijn woord;
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 Ze begonnen in hun tenten te morren, En luisterden niet naar Jahweh’s stem.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Toen stak Hij zijn hand tegen hen op: Hij zou ze neerslaan in de woestijn,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 Hun zaad verstrooien onder de volken, Ze over vreemde landen verspreiden!
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Dan weer koppelden ze zich aan Báal-Peor, En aten de offers van levenloze wezens;
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Ze tergden Hem door hun gedrag, Zodat er een slachting onder hen woedde.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Toen trad Pinechas op, om de misdaad te wreken, En de slachting hield op;
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Het werd hem tot verdienste gerekend, Van geslacht tot geslacht voor altijd.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Ook bij de wateren van Meriba hebben ze Hem getergd, En ging het Moses om hunnentwil slecht:
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Want ze hadden zijn stemming verbitterd, Zodat hem onbezonnen woorden ontsnapten.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Ook verdelgden ze de volkeren niet, Zoals Jahweh het hun had bevolen;
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Maar ze vermengden zich met de heidenen, En leerden hun gewoonten aan:
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Ze vereerden hun beelden, en die werden hun strik;
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Ze brachten hun zonen en dochters aan de goden ten offer;
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Ze gingen onschuldig bloed vergieten, Het bloed van hun zonen en dochters; Ze offerden het aan de beelden van Kanaän, En het land werd door hun bloedschuld ontwijd.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Zo bezoedelden ze zich door eigen maaksels, En dreven overspel met het werk hunner handen!
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Toen werd Jahweh vergramd op zijn volk, En zijn erfdeel begon Hem te walgen:
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Hij leverde ze aan de heidenen uit, En hun haters werden hun meesters;
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Ze werden verdrukt door hun vijand, Moesten bukken onder hun macht.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 En al bracht Hij hun telkens verlossing, Ze bleven in hun opstand volharden! Maar werden ze door hun misdaad vermorzeld,
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Dan zag Hij neer op hun nood, zodra Hij hun smeken vernam;
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Dan was Hij voor hen zijn verbond weer indachtig, Had deernis met hen naar zijn grote ontferming;
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Dan liet Hij hen genade vinden, Bij die hen hadden weggevoerd.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Ach, red ons Jahweh, onze God, En breng ons uit het land der heidenen samen: Opdat wij uw heilige Naam mogen danken, En uw heerlijkheid prijzen!
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Gezegend zij Jahweh, Israëls God, van eeuwigheid tot eeuwigheid! Laat heel het volk het herhalen: Amen! Halleluja!
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalmen 106 >