< Spreuken 31 >

1 Wenken voor Lemoeël, den koning van Massa, die zijn moeder hem gaf.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Mijn zoon, wat zal ik u zeggen; Wat, kind van mijn schoot; Wat, kind van mijn geloften!
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Verkwist uw geld niet aan vrouwen, Schenk uw hart niet aan haar, die koningen verderven;
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Dat past geen koningen, Lemoeël! Het past geen koningen, wijn te drinken; Vorsten mogen niet verzot zijn op drank.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Anders vergeten zij al drinkend de wet, En verdraaien het recht van alle verdrukten.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Geef de drank maar aan hen, die ontredderd zijn, Schenk wijn aan bedroefden:
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Al drinkend vergeten ze hun armoe, En denken niet meer aan hun zorgen.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Kom op voor hen, die niets weten te zeggen, Voor het recht van allen, die verkwijnen;
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Open uw mond, geef een billijk vonnis, Verschaf recht aan armen en tobbers.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Een flinke vrouw! Men vindt haar niet licht; Haar waarde is hoger dan die van juwelen!
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Haar man kan vast op haar bouwen, Hem ontgaat geen winst.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Ze brengt hem voordeel, zolang hij leeft, Nimmer zal ze hem schaden;
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Ze haalt wol en linnen in huis, En verwerkt die met willige handen.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Als een handelsschip haalt ze van verre haar spijs,
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 En als het nog nacht is, staat ze al op, Bereidt ze het eten voor haar gezin, En wijst haar dienstboden de dagtaak aan.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Na rijp beraad koopt ze een akker, Van wat ze verdiende plant ze een wijngaard;
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Ze gordelt haar lenden met kracht, De handen steekt ze uit de mouwen.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Ze onderzoekt, of haar huishouden loopt, Zelfs in de nacht gaat haar lamp niet uit;
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Ze slaat de hand aan het spinnewiel, Haar vingers grijpen de klos.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Ze is vrijgevig voor den arme, Den behoeftige stopt ze iets toe;
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Voor haar gezin hoeft ze de kou niet te vrezen, Want heel haar gezin heeft een dubbel stel kleren.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Zelf maakt ze haar mantels, Ze gaat in lijnwaad en purper gekleed;
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Ook haar man valt op in de poorten, Waar hij zetelt met de oudsten van het land.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Ze verkoopt de eigengemaakte gewaden, En levert den handelaar gordels;
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Ze is met kracht en voornaamheid bekleed, En kent geen angst voor de komende dag.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Haar mond is vol wijsheid, Een vriendelijke wenk ligt op haar tong:
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Zo gaat ze de gangen na van haar gezin, Niet in ledigheid eet ze haar brood!
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Haar zonen staan op, en prijzen haar gelukkig, Haar man ook geeft haar deze lof:
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 "Menige vrouw weert zich dapper, Maar gij hebt ze allen overtroffen!"
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Bedriegelijk is de bevalligheid, en broos is de schoonheid; Maar een vrouw, die Jahweh vreest, blijft geëerd.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Laat haar genieten van wat haar handen wrochtten, In de poorten zullen haar daden haar prijzen!
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Spreuken 31 >