< Zekaria 4 >

1 Malaika mane osebedo kawuoyo koda nochiewa, mana kaka ichiewo ngʼato ma nindo.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 Ne openja niya, “Ineno angʼo?” To ne adwoke niya, “Aneno rachung taya molos gi dhahabu lilo, koket bakul e wiye malo mogik, kod teyni abiriyo maliel, to teynigo nigi kuonde abiriyo mirwakoe kitambi.
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 Bende nitie yiend Zeituni ariyo e bathe, achiel e bath bakul korachwich to machielo e bathe koracham.”
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 Napenjo malaika mane loso kodano niya, “Magi gin angʼo, ruodha?”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 Nodwoka niya, “Ikia gigi adier?” Nadwoke niya, “Ooyo ruodha, akiagi.”
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 Omiyo nowachona niya, “Ma e gima Jehova Nyasaye wacho ne Zerubabel: ‘Ok timre kuom nyalo kata kuom teko, to mana kuom Roho mara,’ Jehova Nyasaye Maratego owacho.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 “Yaye, in got maduongʼ, in to in angʼo? Ibiro pieyi piny michal gi pap e nyim Zerubabel. Bangʼe obiro keto kido mogik mar gedo ka ji kok gimor ni, ‘Nyasaye mondo ogwedh odni! Nyasaye mondo ogwedh odni!’”
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 Wach Jehova Nyasaye nobirona kendo kawacho niya,
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 “Lwet Zerubabel oseketo mise mar hekaluni kendo lwetene ema biro tieke. Eka iningʼe ni Jehova Nyasaye Maratego ema oseora iri.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 “Ngʼa madihedhre chayo odiechieng chako gik matindo? Ji nobed mamor ka gineno tond pimo ot e lwet Zerubabel. “Teyni abiriyogi ochungʼ kar wenge Jehova Nyasaye marango piny koni gi koni.”
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 Eka napenjo malaika niya, “Yiende zeituni ariyo mantie bath rachung taya korachwich gi koracham, to gin angʼo?”
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 Ne achako apenje niya, “Bede ariyo mag yadh zeituni manie bath hotogoro ariyo mag dhahabu ma olo mor dhahabu oko-gi, gin angʼo?”
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 Nodwoka niya, “Ikia gigi adier?” Nawachone niya, “Ooyo ruodha, akiagi.”
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 Eka nokona niya, “Magi e ji ariyo mowir mondo otine Ruoth Nyasaye e piny ngima.”
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”

< Zekaria 4 >