< Zaburi 89 >

1 Maskil mar Ethan ja-Ezra. Abiro wer nyaka chiengʼ kuom (hera) maduongʼ mar Jehova Nyasaye; abiro nyiso ji gi dhoga mi gingʼe kuom adierani e tienge duto.
Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara. Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
2 Abiro nyiso ratiro ni herani ogurore motegno nyaka chiengʼ; kendo ni ne iguro adierani e polo owuon.
Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.
3 Ne iwacho niya, “Asetimo muma gi ngʼata ma ayiero, asesingora ne Daudi jatichna ni,
Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
4 ‘Anachung kothi nyaka chiengʼ kendo anagur lochni motegno e tienge duto.’” (Sela)
‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’” (Sela)
5 Polo pako timbeni miwuoro kod adierani, yaye Jehova Nyasaye, e dier chokruok mar jomaler.
Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
6 Koso en ngʼa e kor polo minyalo pimo gi Jehova Nyasaye? En ngʼa e dier chwech mag polo machalo gi Jehova Nyasaye?
Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
7 E buch jomaler Nyasaye oluor gi luor maduongʼ; olich moloyo chwech duto molwore.
Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
8 Yaye Jehova Nyasaye Maratego en ngʼa machalo kodi? In Jehova Nyasaye iratego kendo adierani olwori.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
9 In giteko ewi nam magingore; ka apakane dhwolore malo, to ikweyogi.
Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
10 Ne ingʼinyo Rahab mana ka kitundu, kendo ne ikeyo wasiki gi badi maratego.
Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
11 Polo gin magi, kendo piny bende en mari. In ema ne imiyo piny obetie kaachiel gi gik moko duto manie iye.
Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
12 Ne ichweyo nyandwat gi milambo; Tabor gi Hermon pako nyingi gi wer gi mor.
Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
13 In-gi bat maratego, lweti bende otegno, kendo lweti ma korachwich nigi duongʼ.
Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
14 Tim makare gi adiera e mise mag lochni; (hera) gi ber otelo e nyimi.
Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
15 Ogwedh joma osepuonjore goyoni sigio mar mor, jogo mawuotho buti e lerni, yaye Jehova Nyasaye.
Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
16 Giil odiechiengʼ duto nikech nyingi; gidhialo timni makare.
Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
17 Nimar in e duongʼgi gi tekogi, kendo isedhialo tungwa kuom ngʼwononi.
Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
18 Adier, kuodi marwa en mar Jehova Nyasaye, ruodhwa en mar Jal Maler mar Israel.
Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
19 Kinde moko ne iwuoyo e yor fweny, mine iwacho ne jogi ma jo-adiera niya, “Asesidho teko kuom jalweny, asemiyo wuowi moro matin duongʼ e dier ji.
Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
20 Aseyudo Daudi jatichna; asewire gi moya maler.
Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
21 Lweta biro sire, adier, bada biro miye teko.
Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
22 Onge ngʼama timbene richo moro amora mane ochune mondo ogolne osuru; onge ngʼama timbene richo moro amora ma nosande.
Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa.
23 Abiro tieko chuth joma kedo kode koneno gi wangʼe, kendo abiro goyo wasike duto piny.
Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye.
24 Herana mar adier nobed kode, kendo tungene nomi duongʼ nikech nyinga.
Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
25 Abiro keyo lwete mi kwak nam, kendo lwete ma korachwich biro kwako aore.
Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje.
26 Obiro luonga ni, ‘In Wuonwa kendo in Nyasacha, lwandana ma Jawarna.’
Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
27 Bende abiro ketone nyathina makayo, ma en Jal motingʼ malo moloyo ruodhi duto mag piny.
Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
28 Abiro siko ka ahere nyaka chiengʼ, kendo winjruok ma atimo kode ok norem mak ochopo ngangʼ.
Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
29 Abiro guro kothe nyaka chiengʼ, kendo lochne nosiki mana kaka polo osiko.
Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
30 “Kata ka yawuote nowe chikna ma ok giluwo yorena,
“Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga,
31 ka ok girito buchena kendo ka chikena otamogi luwo,
ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
32 to anakum richogi gi luth, kendo anago kethogi gi chwat.
Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula.
33 Kata kamano ok anagol herana kuome, bende ok anatimne gima opogore gi adierana.
Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
34 Ok anawe mak achopo winjruokna kode kata loko gima asewacho gi dhoga.
Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
35 Asesingora dichiel kendo mogik kuom ler mara, kendo ok abi riambo ne Daudi,
Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide,
36 ni kothe nodhi nyime nyaka chiengʼ kendo lochne nosiki e nyima ka wangʼ chiengʼ;
kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
37 nogure mi osiki nyaka chiengʼ kaka dwe, ma en ranyisi madier e kor polo.” (Sela)
udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. (Sela)
38 To in isekwedo, kendo iseweya, iyi osewangʼ matek gi ngʼati mowir.
“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
39 Iselokori iweyo singruok mane itimo gi jatichni, kendo isechido osimbone ei buru.
Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
40 Isegoyo ohingane duto piny kendo isemuko kuondege mochiel motegno mi olokore gunda.
Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
41 Ji duto makalo bute oseyake; osedoko ngʼama jobute nyiero.
Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
42 Isetingʼo lwedo ma korachwich mar wasike malo; isemiyo wasike duto oil.
Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere.
43 Bende isemiyo dho liganglane obedo madik kendo ok isekonye e kedo.
Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo.
44 Isemiyo duongʼne orumo kendo isewito lochne piny.
Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
45 Isengʼado ndalo mag tin-ne odoko machiek; isemiyo oneno wichkuot maduongʼ. (Sela)
Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. (Sela)
46 Nyaka karangʼo, yaye Jehova Nyasaye? Ibiro pando wangʼi nyaka chiengʼ koso? Mirimbi biro liel ka mach nyaka karangʼo?
“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
47 Parie kaka ngimana rumo piyo. Neye kaka ne ichweyo dhano duto kayiem!
Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
48 En ngʼa manyalo bedo mangima nyaka chiengʼ mak oneno tho? Koso en ngʼa manyalo resore owuon e teko mar liel? (Sela) (Sheol h7585)
Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol h7585)
49 Yaye Jehova Nyasaye, tinde ere herani maduongʼ machon, (hera) mane isingori kuom adierani, ni initim ne Daudi?
Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
50 Ruoth, parie kaka ji osechayo jatichni, parie kaka atingʼo e chunya ayenje mag ogendini duto,
Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
51 ayenje ma wasiki osejerogo, yaye Jehova Nyasaye, ayenje ma gisejarogo okangʼ kokangʼ mar jatichni mowir.
mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.
52 Opak Jehova Nyasaye nyaka chiengʼ!
“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

< Zaburi 89 >