< Zaburi 71 >

1 Kuomi ema aseponde, yaye Jehova Nyasaye; kik iwe ayud wichkuot.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Konya kendo gola e chandruok, nikech timni makare; winja kendo iresa.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Bedna lwanda mar pondo, ma anyalo ringo adhiye seche duto; gol chik mondo iresa, nimar in e lwandana kendo ohingana.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Resa e lwet joma timbegi richo, yaye Nyasacha, gola kuom richo gi joma kwiny momaka matek.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Nimar in ema isebedo genona, yaye Jehova Nyasaye Manyalo Gik Moko Duto, in ema isebedo kimiya chir nyaka ae tin-na.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 Asebedo ka ayiengora kuomi nyaka ne nywola; in ema ne igola ei minwa. Abiro apaki nyaka chiengʼ.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Alokora gima bwogo ji mangʼeny to kata kamano in e kar pondo mara motegno.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Dhoga opongʼ gi pakni, kendo asiko ahulo duongʼni maler odiechiengʼ duto.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Kik ijog koda ka koro ati; kik ijwangʼa ka tekra orumo.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Nimar wasika wuoyo marach kuoma; jogo marita mondo onega loso wach kaachiel.
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Giwacho niya, “Nyasaye oseweye; laweuru mondo umake, nikech onge ngʼama biro rese.”
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Kik ibed mabor koda, yaye Nyasaye; bi piyo mondo ikonya, yaye Nyasacha.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Mad joma donjona lal nono ka wigi okuot; mad joma dwaro hinya, obed gi achaya kod wichkuot koni gi koni.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Anto abiro siko ka an gi geno; abiro paki kendo abiro medo paki.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Dhoga biro hulo timni makare, kod warruokni odiechiengʼ duto, kata obedo ni gingʼeny mohinga ngʼeyo.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Abiro biro mondo anyis ji timbeni madongo, yaye Jehova Nyasaye Manyalo Gik Moko Duto; abiro nyiso ji timni makare, timni makare in kendi.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Isepuonja nyaka aa e nyathi, yaye Nyasaye, kendo nyaka kawuono pod ahulo timbe miwuoro.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Kata ka ochopo kinde ma ati kendo wiya oselokore lwar, to kik iweya, yaye Nyasaye, nyaka ahul tekoni ni tienge mabiro, kendo ahul timbeni madongo ni tienge duto mabiro.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Timni makare ochopo nyaka ei kor polo, yaye Nyasaye, in misetimo gik madongo. En ngʼa ma dipim kodi, yaye Nyasaye?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Kata obedo ni isemiyo aneno chandruok mathoth kendo malit, to pod ibiro miyo abed mangima kendo. Ibiro gola e bur matut mi achak abed gi duongʼ.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Ibiro miyo duongʼ ma an-go medore kendo ibiro chako ihoya kendo.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Abiro paki gi nyatiti nikech adiera mari, yaye Nyasaye; abiro weroni wend pak gi orutu, yaye Nyasaye Maler mar Israel.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Abiro kok gi mor ka aweroni wend pak, nikech an ngʼat misewaro.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Dhoga biro nyiso ji kuom timbeni makare odiechiengʼ duto, nimar joma ne dwaro hinya oseneno wichkuot kendo osengʼengʼ.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Zaburi 71 >