< Zaburi 69 >

1 Kuom jatend wer e dwol mar “Ondanyo.” Mar Daudi. Resa, yaye Nyasaye, nikech pi oseima nyaka e ngʼuta.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.” Pulumutseni Inu Mulungu, pakuti madzi afika mʼkhosi
2 Asechako nimo e chwodho matut, kama onge lowo motegno ma ngʼato nyalo chungʼie. Asechopo e chuny pi kama tut, kendo apaka olwora oketa diere.
Ine ndikumira mʼthope lozama mʼmene mulibe popondapo. Ndalowa mʼmadzi ozama; mafunde andimiza.
3 Koro aseywak mondo okonya mi aol; dwonda rewni. Wengena pek, ka amanyo Nyasacha.
Ndafowoka ndikupempha chithandizo; kummero kwanga kwawuma gwaa, mʼmaso mwanga mwada kuyembekezera Mulungu wanga.
4 Joma ochaya maonge gima omiyo ngʼeny moloyo yie wiya; joma olokore wasika kayiem thoth adier, jogogo madwaro mondo otieka. Ichuna mondo adwok gima ne ok akwalo.
Iwo amene amadana nane popanda chifukwa ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga; ambiri ndi adani anga popanda chifukwa, iwo amene akufunafuna kundiwononga. Ndikukakamizidwa kubwezera zomwe sindinabe.
5 Ingʼeyo fupa, yaye Nyasaye; kethona ok opondoni.
Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu, kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.
6 Mad joma ogeno kuomi kik ne wichkuot nikech an, yaye Ruoth, Jehova Nyasaye Maratego; mad joma manyi kik ne wichkuot nikech an, yaye Nyasach Israel.
Iwo amene amadalira Inu asanyozedwe chifukwa cha ine, Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Iwo amene amafunafuna Inu asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine, Inu Mulungu wa Israeli.
7 Nimar ji yanya to alingʼ alingʼa nikech in, kendo wichkuot obako lela wangʼa.
Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu, ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.
8 Achalo wendo ne owetena an kaka jamwa ne yawuot minwa;
Ndine mlendo kwa abale anga, munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;
9 nikech (hera) matut ma aherogo odi tieka, kendo ayenje mag joma yanyi lwar kuoma.
pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.
10 Ka aywak kendo atweyo chiemo to pod nyaka ayud ayany;
Pamene ndikulira ndi kusala kudya, ndiyenera kupirira kunyozedwa;
11 ka arwako law ywak, to ji oloka ngero.
pomwe ndavala chiguduli, anthu amandiseweretsa.
12 Joma obet e rangach jara, kendo alokora wer ma jokongʼo wero.
Iwo amene amakhala pa chipata amandinena, ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.
13 To alami, yaye Jehova Nyasaye, e kinde ma iikori mar konya; kuom herani maduongʼ, yaye Nyasaye, dwoka gi resruok mari mar adier.
Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye, pa nthawi yanu yondikomera mtima; mwa chikondi chanu chachikulu Inu Mulungu, mundiyankhe pondipulumutsa.
14 Gola oko e chwodho, kik iyie anim; resa e lwet joma ochaya, gola e chuny pi kama tut.
Mundilanditse kuchoka mʼmatope, musalole kuti ndimire, pulumutseni ine kwa iwo amene amadana nane, kuchoka mʼmadzi ozama.
15 Kik iwe ohula ywera mi tera kata kut mwonya duto, kata bur matut um dhoge ka an e iye.
Musalole kuti chigumula chindimeze, kuya kusandimeze ndipo dzenje lisatseke pakamwa pake kundimiza.
16 Dwoka, yaye Jehova Nyasaye, dwoka, nikech herani ber; lokri ira kuom kechni maduongʼ.
Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu; mwa chifundo chanu chachikulu tembenukirani kwa ine.
17 Kik ipand wangʼi ne jatichni; dwoka piyo, nikech anie chandruok.
Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu, ndiyankheni msanga, pakuti ndili pa mavuto.
18 Bi machiegni mondo ikonya, resa nikech joma kedo koda.
Bwerani pafupi ndi kundilanditsa; ndiwomboleni chifukwa cha adani anga.
19 Ingʼeyo kaka ijara, kaka ikuodo wiya kendo kaka aneno wichkuot; wasika duto ochoma tir.
Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera, kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu.
20 Ajara osechodo chunya kendo aonge gi kar kony. Ne amanyo joma hoya, to ne ok ayudo kata achiel.
Mnyozo waswa mtima wanga ndipo wandisiya wopanda thandizo lililonse; ndinafunafuna ena woti andichitire chisoni, koma panalibe ndi mmodzi yemwe woti anditonthoze, sindinapeze ndi mmodzi yemwe.
21 Negiketo kedhno e chiemba kendo negimiya kong andwayo mondo otiekna riyo.
Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa ndi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu.
22 Mad mesa mochan e nyimgi lokre obadho; kendo mad olokrenegi gir chulo kuor kod otegu.
Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha; chikhale chobwezera chilango ndiponso khwekhwe.
23 Mad wengegi dinre mondo kik ginen kendo oguchgi odolre nyaka chiengʼ.
Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso ndipo misana yawo ipindike mpaka kalekale.
24 Ol mirimbi kuomgi; we mirimbi mager omakgi.
Khuthulirani ukali wanu pa iwo; mkwiyo wanu woyaka moto uwathe mphamvu.
25 Mad miechgi dongʼ gundni; kendo kik iyie ne ngʼato angʼata dag e hembgi.
Malo awo akhale wopanda anthu pasapezeke ndi mmodzi yemwe wokhala mʼmatenti awo.
26 Nimar gisando joma ihinyo kendo giwuoyo kuom lit mag joma ihinyo.
Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulaza ndi kuyankhula zowawa kwa amene munawapweteka.
27 Ket ketho e wigi kuom ketho ka ketho ma gitimo; kendo kik iyie giyud warruok mari.
Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo, musalole kuti akhale ndi gawo pa chipulumutso chanu.
28 Mad ruch kargi oko e kitap joma ngima kendo kik kwan-gi kaachiel gi joma kare.
Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyo ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama.
29 An-gi rem kendo awinjo marach e chunya; mad warruokni rita, yaye Nyasaye.
Ndikumva zowawa ndi kuzunzika; lolani chipulumutso chanu, Inu Mulungu, chinditeteze.
30 Abiro pako nying Nyasaye gi wer kendo abiro miyo nyinge duongʼ gi erokamano.
Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo, ndidzalemekeza Iye ndi chiyamiko.
31 Mano biro miyo Jehova Nyasaye mor moloyo rwadh pur, moloyo rwath mabwoch man-gi tungene kod ombongʼne.
Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe, kupambananso ngʼombe yayimuna, pamodzi ndi nyanga ndi ziboda zake.
32 Joma odhier biro neno mi gibed mamor, un ma udwaro Nyasaye mad chunyu bed mangima!
Wosauka adzaona ndipo adzasangalala, Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo!
33 Jehova Nyasaye winjo joma ochando kendo ok olok ngʼeye ne joge motwe.
Yehova amamvera anthu osowa ndipo sanyoza anthu ake omangidwa.
34 Piny gi polo mondo opake, kaachiel gi nembe kod gik moko duto mawuothoe igi,
Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye, nyanja ndi zonse zomwe zimayenda mʼmenemo,
35 nikech Nyasaye biro reso Sayun kendo obiro gero dala mag Juda kendo. Eka ji nodag kanyo kendo ginikawe kaka margi;
pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni ndi kumanganso mizinda ya Yuda, anthu adzakhala kumeneko ndipo dzikolo lidzakhala lawo;
36 enobed girkeni mar koth jotichne, kendo joma ohero nyinge nodag kanyo.
ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo, ndipo iwo amene amakonda dzina lake adzakhala kumeneko.

< Zaburi 69 >