< Zaburi 57 >

1 Kuom jatend wer. E dwond “Kik iketh gik moko.” Miktam mar Daudi. Kane oringone Saulo mi opondo e rogo. Kecha, yaye Nyasaye, yie ikecha nikech kuomi ema chunya yudoe kar pondo. Abiro pondo e bwo tipo mar bwombeni nyaka chop apaka mager rum.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Aywagora ne Nyasaye Man Malo Moloyo, Nyasaye machopona chenroge ema aywakne.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Ooro wach gie polo kendo oresa, kokwero joma lawa gi tekregi duto; (Sela) Nyasaye oro herane gi adiera mare.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 An e dier sibuoche; anindo e dier le mager mangemo, joma lekegi chalo tonge gi aserni, ma lewgi chalo ligangla mabitho.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Nyingi mondo otingʼ malo moyombo polo, yaye Nyasaye; mad duongʼ mari opongʼ piny duto.
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Ne giyaro jogo mondo omak tiendena, kane chuny lit odola. Ne gikunyo bugo e yora, to kata kamano gin giwegi ema giselutore e iye. (Sela)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Chunya otegno, yaye Nyasaye, chunya otegno; abiro paki gi wer kendo abiro loso wer mamit.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Chiew, in chunya! Chiewuru un orutu gi nyatiti! Abiro chiewo kogwen.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Abiro paki e dier ogendini, yaye Jehova Nyasaye. Abiro werni e dier ogendini.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Nikech herani maduongʼ chopo nyaka e polo; kendo adiera mari chopo nyaka ewi lwasi.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Nyingi mondo otingʼ malo moyombo polo, yaye Nyasaye; mad duongʼ mari opongʼ piny duto.
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Zaburi 57 >