< Zaburi 51 >

1 Kuom jatend wer. Zaburi mar Daudi. Kane janabi Nathan obiro ire bangʼ ka Daudi noseterore gi Bathsheba. Kecha, yaye Nyasaye, kaluwore gi herani ma ok rem; gol kethona duto oko kuom ngʼwononi maduongʼ.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
2 Luok rochruokna duto oko kendo pwodha kuom richona.
Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 Nikech angʼeyo kethona duto kendo richona osiko e nyima.
Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 In iwuon ema asekethoni kendo asetimo richo e nyim wangʼi, mano omiyo in kare ka iwuoyo kendo iwacho adiera ka ingʼadona bura.
Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 En adier chutho ni nonywola e richo asebedo ka an jaricho chakre chiengʼ mane minwa omake ichna.
Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Adier, idwaro ni dhano obed ja-adiera gie chunye iye emomiyo ipuonja rieko gie chunya maiye mogik.
Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Lwoka maler gi owino eka abiro bedo maler; lwoka mondo abed marachar moloyo pe.
Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 We awinjie mor kod ilo; mi chokena misetoyo ochak obedie mamor.
Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Pand wangʼi mondo kik ine richona kendo gol kethona duto oko.
Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 Chwe chuny maler e iya, yaye Nyasaye, kendo los chuny motegno mosiko koluori iket e iya.
Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Kik iriemba buti bende kik igol Roho Maler mari kuoma.
Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Duogna mor ma warruokni kelo kendo mi abed gi chuny mohero timo dwaroni, mondo chuny makamano orita.
Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 Eka abiro puonjo joketho yoreni kendo joricho biro lokore duogo iri.
Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Resa e ketho mar chwero remo, yaye Nyasaye, tim kamano, yaye Nyasaye ma wara, eka lewa biro wer kuom timni makare.
Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Yaye Ruoth yaw pien dhoga, eka dhoga biro hulo pakni.
Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 Ok imor gi misango mitimoni, nikech dine achiwonigo; misango miwangʼo pep ok miyi mor.
Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 Misango mar Nyasaye en chuny motur, chuny motur kendo mamuol, ok itamri, yaye Nyasaye.
Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Mi Sayun odhi maber kuom herani; chak iger ohinga mag Jerusalem kendo.
Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
19 Eka ibiro yudo mor kuom misengni mag joma kare, kuom misango miwangʼo pep mochiw duto, kendo ibiro chiw rwedhi e kendoni mar misango.
Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

< Zaburi 51 >