< Zaburi 43 >

1 Ngʼadna bura makare, yaye Nyasaye, kendo chwaka e kind joma ok ongʼeyo Nyasaye; resa e lwet joma wuondore gi joma timbegi richo.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 In Nyasaye ma apondo kuome. Koro to ijwangʼa nangʼo? Angʼo momiyo nyaka asik ka akuyo, ka jawasigu sanda?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Or lerni kod adierani, orgi mondo gitelna; yie mondo gikela nyaka godi maler, nyaka kama idakie.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Eka anadhi e kendo mar misango mar Nyasaye, nyaka achopi e nyim Nyasaye, Nyasaye ma kelona mor kendo ilo. Abiro paki gi nyatiti, yaye Nyasaye kendo Nyasacha.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Angʼo momiyo ikuyo, yaye chunya? Angʼo momiyo inyosori, yaye chunya? Ket genoni kuom Nyasaye, nikech pod abiro pake, en e Jawarna kendo Nyasacha.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Zaburi 43 >