< Zaburi 25 >

1 Zaburi mar Daudi. Achiwoni chunya, yaye Jehova Nyasaye;
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 In ema aketo genona kuomi, yaye Nyasacha. Kik iwe ane wichkuot, bende kik iwe wasika loya.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Onge ngʼama oketo genone kuomi manyalo neno wichkuot, to joma timo timbe maricho ema biro neno wichkuot.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Nyisa yoreni, yaye Jehova Nyasaye, puonja mondo aluwgi;
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 telna gi adierani, kendo puonja, nikech in Nyasaye ma Jawarna, kendo genona ni kuomi odiechiengʼ duto.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Par kechni maduongʼ gi herani, yaye Jehova Nyasaye, nikech gisebedo ka gintie nyaka aa chon.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Kik ipar richo mane atimo kapod an rawere kod yorena mobam; para kaluwore gi herani, nikech iber, yaye Jehova Nyasaye.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Jehova Nyasaye ber kendo yorene oriere tir; mano emomiyo opuonjo joricho yorene.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Otelo ni joma muol kuom gima nikare kendo opuonjogi yore.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Yore duto mag Jehova Nyasaye opongʼ gihera kod adiera ni joma rito gik moko duto ma singruokne dwaro.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Wena richona nikech nyingi kata obedo ni richona duongʼ ahinya, yaye Jehova Nyasaye,
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Koro ere ngʼat ma oluoro Jehova Nyasaye? Obiro puonje luwo yo moyierne.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Obiro dak e ngima momew, kendo nyikwaye nokaw piny kaka girkeni margi.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Jehova Nyasaye en osiep joma miye luor; omiyo gingʼeyo singruok mage.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Achomo wangʼa kuom Jehova Nyasaye ndalo duto, nikech en kende ema obiro golo tiendena mobadho omako.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Duog ira kendo bedna mangʼwon, nikech adongʼ kenda kendo an gi kuyo.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Chandruok manie chunya osemedore; resa kuom rem ma an-go.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Neye kuyo manie chunya kod rem ma an-go, kendo gol richona duto.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Neye kaka wasika osemedore kendo kaka gichaya gi chunygi duto!
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Rit ngimana kendo iresa; kik iwe ane wichkuot, nikech in ema apondo kuomi.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Mad bidhruok gi ngima moriere rita nikech genona ni kuomi.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Res Israel, yaye Nyasaye, kuom chandruok mage duto!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Zaburi 25 >