< Zaburi 17 >
1 Lamo mar Daudi. Yaye Jehova Nyasaye, yie iwinj kwayona makare; chik iti ne ywakna, chik iti ne lemona, lamona ok aa e dhok mawuondo ji.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Mad chwak michwakago oa kuomi; mad wengeni nee gima kare.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Kata obedo ni inono chunya kendo itema gotieno, kata ka itema to ok ibi yudo gimoro kuoma; asengʼado e chunya ni dhoga ok bi timo richo.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 To kuom gik ma joma moko timo, kaluwore gi wach mowuok e dhogi, an awuon asepogora gi yore jo-mahundu.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Tienda osesiko e yoreni; tiendena pok okier.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Aluongi, yaye Nyasaye, nikech ibiro dwoka; chik iti kendo winj lamona.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Nyisie teko mar herani maduongʼ, in ma ireso ji gi lweti ma korachwich, joma pondo ne wasikgi kuomi.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Rita adimba kaka tong wangʼi, panda e bwo tipo mar bwombi,
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 mondo atony e lwet joma richo ma lawa, mondo atony e lwet wasika ma dhano molwora.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Chunjegi odinore matek, kendo dhogi wuoyo gi wich teko.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Giselawa kuonde duto, mi koro gilwora, ka wengegi ochiek, mondo gidira piny.
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Gichalo sibuor ma nigi kech mar mako le, mana ka sibuor maduongʼ mopondo kokichore.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Aa malo, yaye Jehova Nyasaye, chomgi tir, mi igogi piny; resa e lwet joma richo gi liganglani.
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 Yaye Jehova Nyasaye, resa e lwet joma kamago gi lweti, resa e lwet jopinyni ma pokgi ni e pinyni. Itieko kech ma joma ihero nigo; yawuotgi nigi chiemo mangʼeny, kendo gikano mwandu ne nyithindgi.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 To anane wangʼi ka ngimana nikare; ka achiewo, abiro romo ka aneno kiti kaka ichal.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.