< Ngeche 8 >

1 Donge rieko luongo? Donge ngʼeyo tiend wach tingʼo dwonde ka goyo koko?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Ochungʼ e kuonde motingʼore e bath yo, e akerkeke mag yore.
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Oywak matek e bath dhorangeye midonjogo e dala maduongʼ,
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 kowacho niya, “Aluongou, yaye un ji, aluongou un ji duto manie piny.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Un joma ngʼeyogi tin, nwangʼuru rieko; to un joma ofuwo, nwangʼuru ngʼeyo.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Winjuru, nikech an gi gik mabeyo mangʼeny madwaro nyisou; ayawo dhoga mondo awach gima kare.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Dhoga wacho gima adiera nikech dhoga kwedo gik maricho.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Weche duto mawuok e dhoga gin kare, onge moro kuomgi mobam kata modwanyore.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Ne jogo mongʼeyo pogo tiend wach, gigi duto nikare, giber ni jogo man-gi ngʼeyo.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Yier puonjna kar fedha kendo ngʼeyo kar dhahabu mowal,
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 nikech rieko ber moloyo kite ma nengogi tek, kendo gimoro amora madiher ok nyal romo kode.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 “An, rieko, wadak kaachiel gi ngʼado bura makare; an-gi ngʼeyo kod pogo tiend wach.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Luoro Jehova Nyasaye en sin gi richo; amon gi sunga kod ngʼayi, timbe maricho kod wuoyo mochido.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Ngʼado rieko kod ngʼado bura malongʼo gin maga; an-gi winjo tiend wach kod nyalo.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 An ema amiyo ruodhi locho kendo joloch loso chike makare.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Nikech an, amiyo yawuot ruodhi loch kod joka ruodhi duto marito pinje.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Ahero jogo mohera, to jogo ma manya yuda.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Mwandu gi luor ni kuoma, mwandu mochwere kod mewo.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Olemba ber moloyo dhahabu maber, gino machiwo oloyo fedha moyier.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Awuotho e yo mobidhore makare, e yore mag bura makare,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 kachiwo mwandu ni jogo mohera kendo amiyo kuondegi mag keno bedo mopongʼ chutho.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 “Jehova Nyasaye nokwongo chweya kaka tichne mokwongo motelo ni tijene machon.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 Noyiera aa chakruok manyaka chiengʼ, kapok piny kobetie.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Kapok nembe kobetie, nonywola kata ka sokni mopongʼ gi pi ne onge.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Nonywola ka gode madongo ne pok obedo kuonde ma gintie, bende ka gode matindo ne pod onge,
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 kapok ne ochweyo piny kaachiel gi pewene kata mana lowo mar piny.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Ne antie kane oketo polo kama entie, kata kane oketo giko mar nembe,
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 kane oketo boche polo malo, kendo kane oketo sokni mag nembe mogurore motegno,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 kane ochiwo kuonde giko mag nam matin mondo pi kik okadh kama oketee, kendo kane oloso mise mar piny.
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Ne an jatich molony mobedo bute. Napongʼ gi mor mogundho odiechiengʼ ka odiechiengʼ kamor e nyime kinde duto,
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 ka amor e pinye mangima kendo ail gi ji duto.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 “Omiyo koro yawuota, winjauru; gin johawi jogo morito yorena.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Winjuru puonjna mondo ubed mariek, kik uchagi.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 En jahawi ngʼat mawinja, marito pile e dhoutena korito e dhorangaya.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Nimar ngʼat monwangʼa oyudo ngima kendo oyudo ngʼwono kuom Jehova Nyasaye.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 To ngʼatno ma odaga hinyore kende owuon; jogo duto mamon koda ohero tho.”
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Ngeche 8 >