< Ngeche 26 >

1 Mana kaka pe e ndalo oro kata koth e kinde keyo, e kaka luor ok owinjore ni ngʼat mofuwo.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Mana kaka oyundi mafuyo kata ka opija maringo e kaka kwongʼ maonge gimomiyo kadho akadha.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Kaka faras owinjore gi chwat, to dho punda owinjore gi tweyo e kaka ngʼe joma ofuwo owinjore gi goch.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Kik idwok ngʼat mofuwo machalre gi fupe, to dipo ka ibiro bedo machal kode.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Dwok ngʼat mofuwo koluwore gi fupe, dipo ka obiro nenore e wangʼe owuon ni oriek.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Mana kaka ingʼado tiend ngʼato kata kelo masira, chalo gioro ngʼama ofuwo mondo oter ote.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Mana ka tiend ngʼat mongʼol mawengni, e kaka ngero moa e dho ngʼat mofuwo.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Mana kaka keto kidi e orujre e kaka miyo ngʼat mofuwo luor.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Mana kaka bungu mar kudho e lwet ngʼat momer, e kaka ngero moa e dho ngʼat mofuwo.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Mana kaka ngʼama thoro diro aserni adira ema chalo gi ngʼat mandiko ngʼat mofuwo kata ngʼato angʼata moyudo e tich.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Kaka guok dok e ngʼokne mosengʼogo e kaka ngʼat mofuwo nwoyo fupe.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Bende ineno ngʼato ma paro owuon ni oriek? Ngʼat mofuwo nitiere gi geno moloye.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Jasamuoyo wacho niya, “Sibuor ni e wangʼ yo, sibuor mager bayo e yore mag dala!”
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 Mana kaka dhoot marundore e pata, e kaka jasamuoyo lokore aloka e kitandane.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Jasamuoyo luto lwete malal ei tawo; onyap ahinya ma ok onyal gole oko moduoge e dhoge.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Jasamuoyo paro e chunye ni oriek moloyo ji abiriyo ma dwoko wach gi rieko.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Mana kaka ngʼat mamako guok gi ite, e kaka ngʼat makadho akadha madonjo e dhawo ma ok mare.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Mana kaka ngʼat ma janeko madiro pil mach kata aserni mager,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 e kaka ngʼato mawuondo jabute kowacho niya, “Ne angeri angera!”
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Ka yien onge to mach tho; ka kuoth onge dhawo rumo.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Kaka makaa miyo mach ngʼangʼni, to yien bende miyo mach liel, e kaka ngʼat makwiny kelo miero.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Weche mag kuoth chalo gi chiemo mamit; gidhiyo e chuny dhano ma iye.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Mana kaka range mangʼangʼni mowir e agulu mochwe chalo e kaka lep mager mar chuny mopongʼ gi richo.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Jasigu wuondore koumore kod dhoge, to ei chunye okano miriambo.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Kata bed ni wechene lombo chuny, kik iyie kode, nimar gik maricho abiriyo opongʼo chunye.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Onyalo wuondore ni oonge wuond, to timbene maricho biro nenore ratiro e nyim oganda.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Ka ngʼato okunyo bur, obiro lutore e iye; to ka ngʼato ngʼielo kidi, to kidino biro ngʼielore kaduogo ire.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Lep mariambo mon kod jogo mohinyo, to dhok mawuondo ji kelo kethruok.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Ngeche 26 >