< Ngeche 17 >
1 Ber bangʼo kuon gi kwe kod mor moloyo ot mopongʼ gi chiemo mathoth kod dhawo.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 Misumba mariek biro bedo gi loch kuom wuowi makwodo wich, kendo obiro yudo pok mar girkeni machal mana gi owetene.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 Dhahabu gi fedha itemo gi mach, to Jehova Nyasaye ema temo chuny.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 Ngʼat ma timbene richo chiko ite ne dhok mopongʼ gi richo, ja-miriambo winjo lep mar ajara.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Ngʼat ma jaro jochan ochayo Jachwechgi; ngʼat mamor gi masira ok notony ne kum.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Nyikwayo gin osimbo ne joma oti, to jonywol e mor mar nyithindgi.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Lep mar sunga ok owinjore ne ngʼama ofuwo, to en rach maromo nadi lep mariambo ne jaloch!
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 Asoya en bilo ne ngʼat machiwe, kamoro amora modhiye, odhi maber.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 Ngʼat ma umo ketho mewo hera, to ngʼat mamedo timo gima kamano pogo osiepe moherore.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 Puonj mar kwer konyo ngʼat mariek, moloyo chwat nyadi mia ni ngʼat mofuwo.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Ngʼat ma jaricho ohero mana miero, jaote makwiny ema ibiro orone.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Ber romo gi ondiek madhako moma nyithinde, moloyo romo gi ngʼat mofuwo ei fupe.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Ka ngʼato chulo rach kar ber, rach ok nowe ode.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 Chako dhawo chalo gimuko yawo, emomiyo we wach kapok dhawo owuok.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 Jehova Nyasaye mon-gi ngʼama chwako jaketho kata kumo ngʼat maonge ketho.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Ere tiende mondo ngʼat mofuwo obed gi pesa nimar oonge gi dwaro mar bedo mariek?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 En adier ni osiepni nyalo heri kinde duto, to owadu ema konyi e chandruok.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 Ngʼat maonge gi rieko ema keto gir singo ne jabute.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 Ngʼat mohero dhawo ohero richo; ngʼat mogero ohinga mabor kelo mana hinyruok.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 Ngʼat man-gi chuny marach ok nyal dhi maber; ngʼat ma lewe riambo podho e chandruok.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 Bedo gi ngʼat mofuwo kaka wuowi kelo kuyo; onge mor ni wuoro ma wuon ngʼat mofuwo.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 Chuny mamor en yath maber, to chuny mool tuoyo choke.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 Ngʼat ma timbene richo yie asoya kama opondo mondo oketh gima kare.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Ngʼat mariek keto rieko mondo otel, to wenge ngʼat mofuwo bayo nyaka giko piny.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 Wuowi mofuwo kelo kuyo ni wuon mare kod chuny lit ne ngʼat mane onywole.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Ok en gima ber kumo ngʼat maonge ketho kata goyo joote nikech dimbruokgi.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 Ngʼat man-gi ngʼeyo konyore gi weche kotangʼ; to ngʼat man-gi winjo wach to ritore maber.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Kata ngʼat mofuwo ikwano ka ngʼat mariek ka olingʼ thi; kendo ka ngʼat mongʼeyo ka orito lewe.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.